Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Luka 1:12 - Buku Lopatulika

Ndipo Zekariya anadabwa pamene anamuona, ndipo mantha anamgwira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Zekariya anadabwa pamene anamuona, ndipo mantha anamgwira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Zakariya adadzidzimuka pomuwona, nachita mantha.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.

Onani mutuwo



Luka 1:12
9 Mawu Ofanana  

Ndipo ine Daniele ndekha ndinaona masomphenyawo; pakuti anthu anali nane sanaone masomphenyawo; koma kunawagwera kunjenjemera kwakukulu, nathawa kubisala.


Ndipo pamene analowa m'manda, anaona mnyamata alikukhala kumbali ya kudzanja lamanja, wovala mwinjiro woyera; ndipo iwo anadabwa.


Koma iye ananthunthumira ndi mau awa, nasinkhasinkha kulonjera uku nkutani.


Ndipo pompenyetsetsa iye ndi kuopa, anati, Nchiyani, Mbuye? Ndipo anati kwa iye, Mapemphero ako ndi zachifundo zako zinakwera zikhala chikumbutso pamaso pa Mulungu.


Ndipo pamene ndinamuona Iye, ndinagwa pa mapazi ake ngati wakufa; ndipo anaika dzanja lake lamanja pa ine, nati, Usaope, Ine ndine Woyamba ndi Wotsiriza,


Nati Manowa kwa mkazi wake, Tidzafa ndithu pakuti taona Mulungu.


Pamenepo Gideoni anaona kuti ndiye mthenga wa Yehova, nati Gideoni, Tsoka ine, Yehova Mulungu! Popeza ndaona mthenga wa Yehova maso ndi maso.