Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 7:10 - Buku Lopatulika

Ndipo panali pamene anapita masiku asanu ndi awiri, madzi a chigumula anali padziko lapansi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo panali pamene anapita masiku asanu ndi awiri, madzi a chigumula anali pa dziko lapansi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Patangopita masiku asanu ndi aŵiri, chigumula chidafika pa dziko lonse lapansi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.

Onani mutuwo



Genesis 7:10
7 Mawu Ofanana  

Ndine, taonani, ndipo Ine ndidzadzetsa chigumula cha madzi padziko lapansi, kuti chiononge zamoyo zonse, m'mene muli mpweya wa moyo pansi pathambo; zinthu zonse za m'dziko lapansi zidzafa.


Pakuti akapita masiku asanu ndi awiri Ine ndidzavumbitsa mvula padziko lapansi masiku makumi anai usana ndi usiku; ndi zinthu zamoyo zonse zomwe ndazipanga ndidzaziononga padziko lapansi.


zinalowa ziwiriziwiri kwa Nowa m'chingalawamo, yamphongo ndi yaikazi, monga momwe Mulungu anamlamulira Nowa.


Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao, chigumula chinakokolola kuzika kwao;


Anadya, anamwa, anakwatira, anakwatiwa, kufikira tsiku lija Nowa analowa m'chingalawa, ndipo chinadza chigumula, nkuwaononga onsewo.