Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 50:1 - Buku Lopatulika

Ndipo Yosefe anagwa pa nkhope ya atate wake, namlirira iye nampsompsona iye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Yosefe anagwa pa nkhope ya atate wake, namlirira iye nampsompsona iye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pomwepo Yosefe adadzigwetsa pa mtembo wa bambo wake akulira, kwinaku akumpsompsona bambo wake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.

Onani mutuwo



Genesis 50:1
11 Mawu Ofanana  

Ndipo Sara anafa mu Kiriyati-Ariba (ndiwo Hebroni), m'dziko la Kanani; ndipo Abrahamu anadza ku maliro a Sara, kuti amlire.


Ine ndidzatsikira pamodzi ndi iwe ku Ejipito; ndipo Ine ndidzakubwezanso ndithu; ndipo Yosefe adzaika dzanja lake pamaso pako.


Pamene Yakobo anatha kulangiza ana ake aamuna, anafunya mapazi ake pakama, natsirizika, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wake.


Ndipo Yosefe anauza akapolo ake asing'anga kuti akonze atate wake ndi mankhwala osungira thupi: ndipo asing'anga anakonza Israele.


Ndipo Elisa anadwala nthenda ija adafa nayo, namtsikira Yehowasi mfumu ya Israele, namlirira, nati, Atate wanga, atate wanga, galeta wa Israele ndi apakavalo ake!


Ndipo anamuika Stefano anthu opembedza, namlira maliro aakulu.


Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi chilangizo cha Ambuye.


Koma sitifuna, abale, kuti mukhale osadziwa za iwo akugona; kuti mungalire monganso otsalawo, amene alibe chiyembekezo.