Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti

- Zotsatsa -




Genesis 49:33 - Buku Lopatulika

33 Pamene Yakobo anatha kulangiza ana ake aamuna, anafunya mapazi ake pakama, natsirizika, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

33 Pamene Yakobo anatha kulangiza ana ake amuna, anafunya mapazi ake pakama, natsirizika, nasonkhanizidwa kwa anthu a mtundu wake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

33 Tsono Yakobe atamaliza kulangiza ana ake, adabwezeranso mapazi ake m'bedi ndipo adamwalira.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 49:33
22 Mawu Ofanana  

Ndipo anamtulutsa iye kunja, nati, Tayang'anatu kumwamba, uwerenge nyenyezi, ngati ukhoza kuziwerenga zimenezo: ndipo anati kwa iye, Zoterezo zidzakhala mbeu zako.


Zaka za moyo wa Ismaele ndi izi: zaka zana limodzi kudza makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri: ndipo iye anamwalira, natengedwa akhale ndi a mtundu wake.


Ndipo Abrahamu anamwalira, nafa mu ukalamba wake wabwino, nkhalamba ya zaka zambiri; natengedwa akhale ndi a mtundu wake.


Ndipo Isaki anatsirizika nafa, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wake, wokalamba ndi wa masiku okwanira: ndipo Esau ndi Yakobo ana ake aamuna anamuika iye.


Ndipo Yakobo anaitana ana ake aamuna, nati, Sonkhanani inu, kuti ndikuuzeni inu chimene chidzakugwerani inu masiku akudzawo.


Ndipo analangiza iwo nati kwa iwo, Ine nditi ndisonkhanitsidwe kwa anthu a mtundu wanga; mundiike ine pamodzi ndi makolo anga m'phanga lili m'munda wa Efuroni Muhiti,


munda ndi phanga lili m'menemo, zinagulidwa kwa ana a Hiti


Ndipo Yosefe anagwa pa nkhope ya atate wake, namlirira iye nampsompsona iye.


Ndipo Elisa anadwala nthenda ija adafa nayo, namtsikira Yehowasi mfumu ya Israele, namlirira, nati, Atate wanga, atate wanga, galeta wa Israele ndi apakavalo ake!


Pamenepo Elisa anamwalira, ndipo anamuika. Ndipo magulu a Amowabu analowa m'dziko poyambira chaka.


Koma munthu akufa atachita liondeonde inde, munthu apereka mzimu wake, ndipo ali kuti?


Pakuti ndidziwa kuti mudzandifikitsa kuimfa, ndi kunyumba yokomanamo amoyo onse.


Udzafika kumanda utakalamba, monga abwera nao mtolo wa tirigu m'nyengo yake.


fumbi ndi kubwera pansi pomwe linali kale, mzimu ndi kubwera kwa Mulungu amene anaupereka.


Tsopano, Ambuye, monga mwa mau anu aja, lolani ine, kapolo wanu, ndichoke mumtendere;


Ndipo Yakobo anatsikira ku Ejipito; ndipo anamwalira, iye ndi makolo athu;


Ndi chikhulupiriro, Yosefe, pakumwalira, anatchula za matulukidwe a ana a Israele; nalamulira za mafupa ake.


ndi kwa msonkhano wa onse ndi Mpingo wa obadwa oyamba olembedwa mu Mwamba, ndi kwa Mulungu Woweruza wa onse, ndi kwa mizimu ya olungama oyesedwa angwiro,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa