Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 42:10 - Buku Lopatulika

Ndipo iwo anati kwa iye, Iai, mbuyanga, koma akapolo anu adzera kudzagula chakudya.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo iwo anati kwa iye, Iai, mbuyanga, koma akapolo anu adzera kudzagula chakudya.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Iwo aja adayankha kuti, “Iyai mbuyathu, ife atumiki anu tabwera kuti tidzagule chakudya basi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya.

Onani mutuwo



Genesis 42:10
7 Mawu Ofanana  

Anthu akutumikire iwe, mitundu ikuweramire iwe; uchite ufumu pa abale ako, ana a amai ako akuweramire iwe. Wotemberereka aliyense akutemberera iwe, wodalitsika aliyense akudalitsa iwe.


Ndipo anayankha Isaki nati kwa Esau, Taona, ndamuyesa iye mkulu wako, ndi abale ake onse ndampatsa iye akhale akapolo ake; ndakhazikitsa iye ndi tirigu ndi vinyo; nanga pamenepo mwana wanga, ndidzakuchitira iwe chiyani?


Abale ake ndipo anati kwa iye, Kodi udzakhala mfumu yathu ndithu? Kapena udzatilamulira ife ndithu kodi? Ndipo anamuda iye koposa chifukwa cha maloto ake ndi mau ake.


Tonse tili ana aamuna a munthu mmodzi; tili oona, akapolo anu, sitili ozonda.


Iye wa akapolo anu ampeza nacho afe, ndipo ifenso tidzakhala akapolo a mbuyanga.


Ndipo Obadiya ali m'njira taona, Eliya anakomana naye; iye namdziwa, namgwadira, nati, Ndinu kodi mbuye wanga Eliya?


Ndipo Saulo anazindikira mau ake a Davide, nati, Ndi mau ako awa, mwana wanga Davide? Nati Davide, Ndi mau anga mfumu, mbuye wanga.