Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 26:32 - Buku Lopatulika

Ndipo panali tsiku lomwelo anyamata ake a Isaki anadza namuuza iye za chitsime chimene anakumba, nati kwa iye, Tapeza madzi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo panali tsiku lomwelo anyamata ake a Isaki anadza namuuza iye za chitsime chimene anakumba, nati kwa iye, Tapeza madzi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsiku limenelo antchito ake a Isaki adabwera kudzamuuza za chitsime chimene iwowo adaakumba. Adati, “Tapeza madzi.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tsiku limenelo, antchito a Isake anabwera namuwuza za chitsime chimene anakumba. Iwo anati, “Tawapeza madzi!”

Onani mutuwo



Genesis 26:32
7 Mawu Ofanana  

Ndipo anamanga kumeneko guwa la nsembe, naitana dzina la Yehova, namanga hema wake kumeneko: ndi pamenepo anyamata a Isaki anakumba chitsime.


Ndipo analawira m'mamawa nalumbirirana wina ndi mnzake; ndipo Isaki anawalola amuke, ndipo anauka kuchokera kwa iye m'mtendere.


Ndipo anatcha dzina lake Siba, chifukwa chake dzina la mzindawo ndi Beereseba kufikira lero lino.


Wochita ndi dzanja laulesi amasauka; koma dzanja la akhama lilemeretsa.


Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu; koma moyo wa akhama udzalemera.


Pemphani, ndipo chidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo chidzatsegulidwa kwa inu;