Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 24:6 - Buku Lopatulika

Ndipo Abrahamu anati kwa iye, Chenjera iwe, usambwezerenso mwana wanga kumeneko.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Abrahamu anati kwa iye, Chenjera iwe, usambwezerenso mwana wanga kumeneko.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Abrahamu adayankha kuti, “Usadzamperekeze kumeneko mwana wangayo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.

Onani mutuwo



Genesis 24:6
7 Mawu Ofanana  

Ndipo anati kwa iye mnyamatayo, Kapena sadzafuna mkaziyo kunditsata ine ku dziko lino: kodi ndikambwezerenso mwana wanu ku dziko komwe mwachokera inu?


Ndipo ngati sadzafuna mkaziyo kukutsata iwe, udzakhala wosachimwa pa chilumbiro changachi: koma mwana wanga usambwezerenso kumeneko.


Khristu anatisandutsa mfulu, kuti tikhale mfulu; chifukwa chake chilimikani, musakodwenso ndi goli la ukapolo.


Koma ife si ndife a iwo akubwerera kulowa chitayiko; koma a iwo a chikhulupiriro cha ku chipulumutso cha moyo.


Ndi chikhulupiriro anakhala mlendo kudziko la lonjezano, losati lake, nakhalira m'mahema pamodzi ndi Isaki ndi Yakobo, olowa nyumba pamodzi ndi iye a lonjezano lomwelo;