Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 8:31 - Buku Lopatulika

Ndipo Yehova anachita monga mwa mau a Mose; nachotsera Farao ndi anyamata ake ndi anthu ake mizazayo, sunatsale ndi umodzi wonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Yehova anachita monga mwa mau a Mose; nachotsera Farao ndi anyamata ake ndi anthu ake mizazayo, sunatsala ndi umodzi wonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Motero Chauta adachitadi monga momwe Mose adapemphera. Pomwepo mizaza idamchoka Farao ndi nduna zake ndi anthu ake omwe. Sudatsalepo ndi umodzi omwe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala.

Onani mutuwo



Eksodo 8:31
5 Mawu Ofanana  

Anapatuka onse; pamodzi anavunda mtima; palibe wakuchita bwino ndi mmodzi yense.


Pakuti ukapanda kulola anthu anga amuke, taona, ndidzatuma mizaza pa iwe, ndi pa anyamata ako, ndi pa anthu ako, ndi pa nyumba zako; ndipo nyumba za Aejipito zidzadzala nayo mizaza, ndi nthaka yomwe imene ikhalapo.


Ndipo Mose anatuluka kwa Farao, napemba Yehova.


Koma Farao anaumitsa mtima wake nthawi yomweyonso, ndipo sanalole anthu amuke.


Ungayanje woipa, koma sadzaphunzira chilungamo; m'dziko la machitidwe oongoka, iye adzangochimwa, sadzaona chifumu cha Yehova.