Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 5:7 - Buku Lopatulika

Musawapatsanso anthu udzu wakupanga nao njerwa monga kale; apite okha adzifunire udzu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Musawapatsanso anthu udzu wakupanga nao njerwa monga kale; apite okha adzifunire udzu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Musaŵapatsenso udzu wa njerwa anthu ameneŵa, monga muja munkachitiramu. Alekeni azikamweta okha udzuwo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo.

Onani mutuwo



Eksodo 5:7
5 Mawu Ofanana  

Ndipo ananenana wina ndi wina, Tiyeni tipange njerwa, tiziotchetse. Ndipo anali ndi njerwa naziyesa miyala, ndi katondo anayesa matope.


Natinso kwa iye, Tili nao udzu ndi zakudya zambiri ndi malo ogona.


Ndipo tsiku lomwelo Farao analamulira akufulumiza anthu, ndi akapitao ao, ndi kuti,


Ndipo muziwawerengera njerwa, monga momwe anapanga kale; musachepsapo, popeza achita ulesi; chifukwa chake alikufuula, ndi kuti, Timuke, timphere nsembe Mulungu wathu.


Ngakhale udzu ndi chakudya cha abulu athu ziliko; ndi mkate ndi vinyo zilikonso kwa ine ndi kwa mdzakazi wako ndi kwa mnyamata wokhala ndi akapolo ako; kosasowa kanthu.