Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 39:4 - Buku Lopatulika

Anapangira efodi zapamapewa zolumikizana; pansonga ziwirizo anamlumikiza.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Anapangira efodi zapamapewa zolumikizana; pa nsonga ziwirizo anamlumikiza.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono adapanga tizikwewo tam'mapewa ta chovala cha efodi chija, tolumikizika ku chovalacho pa mbali zake ziŵiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo anapanga efodi imene inali ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa, tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.

Onani mutuwo



Eksodo 39:4
4 Mawu Ofanana  

Koma nsonga zake ziwiri za maunyolo opotawo uzimange ku zoikamo ziwiri, ndi kuziika pa zapamapewa ziwiri za efodi, m'tsogolo mwake.


Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zake ziwiri, kuti amangike nazo.


Ndipo anasula golide waphanthiphanthi, nalemba nsambo, kuti amuombe pamodzi ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ntchito ya m'misiri.


Ndi mpango wa efodi wokhala pamenepo, wakummanga nao unali woombera kumodzi wa chiombedwe chomwechi; wa golide, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa; monga Yehova adauza Mose.