Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 27:18 - Buku Lopatulika

Utali wake wa bwalolo ukhale wa mikono zana limodzi, ndi kupingasa kwake makumi asanu monsemo, ndi msinkhu wake wa mpanda mikono isanu; ukhale wabafuta wa thonje losansitsa; ndi makamwa a nsichizo akhale amkuwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Utali wake wa bwalolo ukhale wa mikono zana limodzi, ndi kupingasa kwake makumi asanu monsemo, ndi msinkhu wake wa mpanda mikono isanu; ukhale wabafuta wa thonje losansitsa; ndi makamwa a nsichizo akhale amkuwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kutalika kwake kwa bwalolo kukhale mamita 46, muufupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu zochingazo zikhale za thonje losankhidwa bwino kwambiri ndi lopikidwa, ndipo masinde ake akhale amkuŵa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kutalika kwa bwalolo kukhale mamita 46, mulifupi mwake mamita 23, msinkhu wake masentimita 230. Nsalu ya katani ikhale yofewa ndi yosalala bwino. Matsinde ake akhale amkuwa.

Onani mutuwo



Eksodo 27:18
3 Mawu Ofanana  

Ndipo uzipanga chihema ndi nsalu zophimba khumi, za bafuta wa thonje losansitsa, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira; uombemo akerubi, ntchito ya mmisiri.


Nsichi zonse za pabwalo pozungulira zimangike pamodzi ndi mitanda yasiliva; zokowera zao zasiliva, ndi makamwa ao amkuwa.


Zipangizo zonse za chihema, m'machitidwe ake onse, ndi zichiri zake zonse, ndi zichiri zonse za bwalo lake, zikhale zamkuwa.