Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 26:5 - Buku Lopatulika

Uziika magango makumi asanu pansalu yochingira imodzi, nuikenso magango makumi asanu m'mphepete mwake mwa nsalu ya chilumikizano china; ndipo magango akomanizane lina ndi linzake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Uziika magango makumi asanu pa nsalu yochingira imodzi, nuikenso magango makumi asanu m'mphepete mwake mwa nsalu ya chilumikizano china; ndipo magango akomanizane lina ndi linzake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kenaka upange timagonga makumi asanu pa nsalu yoyambayo, ndipo timagonga tinanso makumi asanu pa nsalu yachiŵiriyo, kuti timagongato tiyang'anane.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.

Onani mutuwo



Eksodo 26:5
3 Mawu Ofanana  

Ndipo uziika magango a nsalu ya madzi m'mphepete mwake mwa nsalu imodzi, ku mkawo wa chilumikizano; nuchite momwemo m'mphepete mwake mwa nsalu ya kuthungo ya chilumikizano china.


Uzipanganso zokowera makumi asanu zagolide, ndi kumanga nsaluzo pamodzi ndi zokowerazo; kuti chihema chikhale chimodzi.


Anaika magango makumi asanu pansalu imodzi, naikanso magango makumi asanu m'mphepete mwake mwa nsalu ya chilumikizano china; magango anakomanizana lina ndi linzake.