Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 26:17 - Buku Lopatulika

Pa thabwa limodzi pakhale mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; uzitero pa matabwa onse a chihema.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pa thabwa limodzi pakhale mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; uzitero pa matabwa onse a Kachisi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziŵiri, ndipo mafulemu onse a chihemacho apangidwe ndi matabwa otere.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.

Onani mutuwo



Eksodo 26:17
5 Mawu Ofanana  

Utali wake wa thabwa limodzi ndiwo mikono khumi, ndi kupingasa kwake kwa thabwali mkono ndi hafu.


Ndipo uzipanga matabwa a chihema, matabwa makumi awiri ku mbali ya kumwera, kumwera.


Nuzipanga makamwa makumi anai asiliva pansi pa matabwa makumi awiri; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi kwa mitsukwa yake iwiri, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina kwa mitsukwa yake iwiri;


Pa thabwa limodzi panakhala mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; anawapanga momwemo matabwa onse a chihema.


napanga makamwa makumi anai asiliva pansi pa matabwa makumi awiri; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi kwa mitsukwa yake iwiri, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina kwa mitsukwa yake iwiri.