Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 12:24 - Buku Lopatulika

Ndipo muzisunga chinthu ichi chikhale lemba la kwa inu, ndi kwa ana anu ku nthawi zonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo muzisunga chinthu ichi chikhale lemba la kwa inu, ndi kwa ana anu ku nthawi zonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Muziŵamvera malamulo ameneŵa inuyo ndi ana anu mpaka muyaya.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.

Onani mutuwo



Eksodo 12:24
6 Mawu Ofanana  

Ndipo tsiku lino lidzakhala kwa inu chikumbutso, muzilisunga la chikondwerero cha Yehova; ku mibadwo yanu muzilisunga la chikondwerero, likhale lemba losatha.


Ndipo muzisunga chikondwerero cha Mkate wopanda chotupitsa; pakuti tsiku lomwe lino ndinatulutsa makamu anu m'dziko la Ejipito; chifukwa chake muzisunga tsiku lino m'mibadwo yanu, lemba losatha.


Ndipo kudzakhala, pamene mulowa m'dziko limene Yehova adzakupatsani, monga analankhula, muzisunga kutumikira kumeneku.


Chifukwa chake uzikasunga lemba ili pa nyengo yake chaka ndi chaka.


Ndipo kudzakhala atakulowetsa Yehova m'dziko la Akanani, ndi la Ahiti, ndi la Aamori ndi la Ahivi, ndi la Ayebusi, limene analumbira ndi makolo ako kukupatsa, m'dziko moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi, uzikasunga kutumikira kumeneku mwezi uno.