Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Akolose 1:8 - Buku Lopatulika

amenenso anatifotokozera chikondi chanu mwa Mzimu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

amenenso anatifotokozera chikondi chanu mwa Mzimu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndiye amene adatidziŵitsa za chikondi chomwe Mzimu Woyera adaika mwa inu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.

Onani mutuwo



Akolose 1:8
7 Mawu Ofanana  

Pakuti kulibe kanthu kobisika, koma kuti kaonetsedwe; kapena kulibe kanthu kanakhala kam'tseri, koma kuti kakaululidwe.


Ndipo ndikudandaulirani, abale, ndi Ambuye wathu Yesu Khristu, ndi chikondi cha Mzimu, kuti mudzalimbike pamodzi ndi ine m'mapemphero anu kwa Mulungu chifukwa cha ine;


ndipo chiyembekezo sichichititsa manyazi; chifukwa chikondi cha Mulungu chinatsanulidwa m'mitima mwathu mwa Mzimu Woyera, amene wapatsidwa kwa ife.


Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,


popeza tidamva za chikhulupiriro chanu cha mwa Khristu Yesu, ndi chikondi muli nacho kwa oyera mtima onse;


Pakuti Mulungu sanatipatse mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi chikondi ndi chidziletso.


Popeza mwayeretsa moyo wanu pakumvera choonadi kuti mukakonde abale ndi chikondi chosanyenga, mukondane kwenikweni kuchokera kumtima;