Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 5:22 - Buku Lopatulika

Ndipo Afilisti anakweranso kachiwiri, natanda m'chigwa cha Refaimu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Afilisti anakweranso kachiwiri, natanda m'chigwa cha Refaimu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nthaŵi ina Afilisti adabweranso, nandanda m'chigwa chija cha Refaimu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nthawi inanso Afilisti anabweranso namwazikana mʼChigwa cha Refaimu;

Onani mutuwo



2 Samueli 5:22
7 Mawu Ofanana  

Ndipo Afilisti anaponyananso nkhondo ndi Aisraele; ndipo Davide anatsika ndi anyamata ake pamodzi naye naponyana ndi Afilisti; nafuna kukomoka Davide.


Ndipo atatu a mwa makamu atatu opambanawo, anatsika nafika kwa Davide nyengo ya kukolola m'phanga la ku Adulamu; ndi gulu la Afilisti linamanga zithando m'chigwa cha Refaimu.


Tsono Afilisti anafika natanda m'chigwa cha Refaimu.


Ndipo mneneri uja anayandikira kwa mfumu ya Israele, nati kwa iye, Kadzilimbitseni, mudziwe muchenjere ndi chimene muchichita; popeza chaka chikudzachi mfumu ya Aramu idzabweranso kulimbana nanu.


Ndipo Afilisti anabwerezanso, nafalikira m'chigwamo.


Ndipo padzakhala ngati wamasika alikumweta tirigu wosacheka, ndi dzanja lake lilikudula ngala; inde padzakhala ngati pamene wina akunkha ngala m'chigwa cha Refaimu.


nakwera malire kunka ku chigwa cha mwana wa Hinomu, kumbali kwa Ayebusi, kumwera, ndiko Yerusalemu; nakwera malire kunka kumwamba kwa phiri lokhala patsogolo pa chigwa cha Hinomu kumadzulo, ndilo ku mathero ake a chigwa cha Refaimu kumpoto.