2 Samueli 5:13 - Buku Lopatulika Ndipo Davide anadzitengera akazi aang'ono ena ndi akazi a ulemu ena a ku Yerusalemu, atafikako kuchokera ku Hebroni; ndipo anambadwira Davide ana aamuna ndi aakazi. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo Davide anadzitengera akazi aang'ono ena ndi akazi a ulemu ena a ku Yerusalemu, atafikako kuchokera ku Hebroni; ndipo anambadwira Davide ana aamuna ndi aakazi. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Tsono Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, adakwatira akazi ena natenganso azikazi ena kumeneko. Tsono adabereka ana ambiri, aamuna ndi aakazi. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Davide atafika ku Yerusalemu kuchokera ku Hebroni, anakwatira azikazi natenganso akazi ena kumeneko, ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri. |
Ndipo Davide anazindikira kuti Yehova anamkhazikitsa mfumu ya Israele, ndi kuti anakulitsa ufumu wake chifukwa cha anthu ake Israele.
Ndipo anali nao akazi mazana asanu ndi awiri, ana aakazi a mafumu, ndi akazi aang'ono mazana atatu; ndipo akazi ake anapambutsa mtima wake.
Ana a Davide tsono ombadwira ku Hebroni: woyamba Aminoni wa Ahinowamu wa ku Yezireele, wachiwiri Daniele wa Abigaile wa ku Karimele,
Onsewa ndiwo ana a Davide, pamodzi ndi ana a akazi aang'ono; ndipo Tamara ndiye mlongo wao.
Koma Abiya anakula mphamvu, nadzitengera akazi khumi ndi anai, nabala ana aamuna makumi awiri mphambu awiri, ndi ana aakazi khumi mphamvu asanu ndi mmodzi.
Ndipo asadzichulukitsire akazi, kuti ungapatuke mtima wake; kapena asadzichulukitsire kwambiri siliva ndi golide.