Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 24:19 - Buku Lopatulika

Ndipo Davide anakwerako monga mwa kunena kwa Gadi, monga adalamulira Yehova.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Davide anakwerako monga mwa kunena kwa Gadi, monga adalamulira Yehova.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Atamva mau a Gadiwo, Davide adapita monga momwe Chauta adaalamulira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.

Onani mutuwo



2 Samueli 24:19
8 Mawu Ofanana  

Chotero anachita Nowa, monga mwa zonse anamlamulira iye Mulungu, momwemo anachita.


Ndipo Gadi anafika tsiku lomwelo kwa Davide nanena naye, Kwerani mukamangire Yehova guwa la nsembe pa dwale la Arauna Myebusi.


Ndipo Arauna anayang'ana naona mfumuyo ndi anyamata ake alikubwera kwa iye; natuluka Arauna naweramira pamaso pa mfumu nkhope yake pansi.


Ndipo Davide anakwera monga mwa mau a Gadi adawanena m'dzina la Yehova.


Nalawira mamawa, natuluka kunka kuchipululu cha Tekowa; ndipo potuluka iwo, Yehosafati anakhala chilili, nati, Mundimvere ine, Ayuda inu, ndi inu okhala mu Yerusalemu, limbikani mwa Yehova Mulungu wanu, ndipo mudzakhazikika; khulupirirani aneneri ake, ndipo mudzalemerera.


koma ananyodola mithenga ya Mulungu, napeputsa mau ake, naseka aneneri ake, mpaka ukali wa Yehova unaukira anthu ake, mpaka panalibe cholanditsa.


Koma anakhala osamvera, napandukira Inu, nataya chilamulo chanu m'mbuyo mwao napha aneneri anu akuwachitira umboni, kuwabwezera kwa Inu, nachita zopeputsa zazikulu.


Ndi chikhulupiriro Abrahamu, poitanidwa, anamvera kutuluka kunka kumalo amene adzalandira ngati cholowa; ndipo anatuluka wosadziwa kumene akamukako.