Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 19:2 - Buku Lopatulika

Ndipo chipulumutso cha tsiku lija chinasandulika maliro kwa anthu onse; pakuti anthu anamva kuti, Mfumu ili ndi chisoni chifukwa cha mwana wake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo chipulumutso cha tsiku lija chinasandulika maliro kwa anthu onse; pakuti anthu anamva kuti, Mfumu ili ndi chisoni chifukwa cha mwana wake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho chikondwerero cha tsikulo chidasanduka maliro kwa anthu onse, pakuti anthu adamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo kwa asilikali onse chipambano cha tsiku limenelo chinasandulika maliro, chifukwa tsiku limenelo anthu anamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.

Onani mutuwo



2 Samueli 19:2
5 Mawu Ofanana  

Ndipo Yowabu mwana wa Zeruya anazindikira kuti mtima wa mfumu unalunjika kwa Abisalomu.


Ndipo anauza Yowabu, Onani mfumu ilikulira misozi, nilira Abisalomu.


Ndipo tsiku lija anthu analowa m'mzinda kachetechete, monga azemba anthu akuchita manyazi pakuthawa nkhondo.


M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo; kukoma mtima kwake kunga mtambo wa mvula ya masika.


Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango; koma kukoma mtima kwake kunga mame pamsipu.