Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 1:18 - Buku Lopatulika

nawauza aphunzitse ana Ayuda nyimbo iyi ya Uta, onani inalembedwa m'buku la Yasara,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

nawauza aphunzitse ana Ayuda nyimbo iyi ya Uta, onani inalembedwa m'buku la Yasara,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo adalamula kuti mau a madandaulowo aŵaphunzitse kwa anthu a ku Yuda. Mau ake ndi aŵa, monga adalembedwera m'buku la Yasara.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:

Onani mutuwo



2 Samueli 1:18
4 Mawu Ofanana  

Yuda, abale ako adzakuyamika iwe; dzanja lako lidzakhala pa khosi la adani ako; ana aamuna a atate wako adzakuweramira.


Ulemerero wako, Israele, unaphedwa pa misanje yako. Ha! Adagwa amphamvu!


Tsikuli munaima pamaso pa Yehova Mulungu wanu mu Horebu muja Yehova anati kwa ine, Ndisonkhanitsire anthu, ndidzawamvetsa mau anga, kuti aphunzire kundiopa Ine masiku ao onse akukhala ndi moyo padziko lapansi, ndi kuti aphunzitse ana ao.


Ndipo dzuwa linalinda, ndi mwezi unaima mpaka anthu adabwezera chilango adani ao. Kodi ichi sichilembedwa m'buku la Yasara? Ndipo dzuwa linakhala pakati pa thambo, losafulumira kulowa ngati tsiku lamphumphu.