Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Akorinto 10:11 - Buku Lopatulika

Woteroyo ayese ichi kuti monga tili ife ndi mau mwa makalata, pokhala palibe ife, tili oterenso m'machitidwe pokhala tili pomwepo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Woteroyo ayese ichi kuti monga tili ife ndi mau mwa akalata, pokhala palibe ife, tili oterenso m'machitidwe pokhala tili pomwepo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu oganiza zotere, adziŵe kuti palibe kusiyana pakati pa zimene timanena m'makalata pamene tili nanu kutali ndi zimene timachita tikakhala nanu pamodzi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.

Onani mutuwo



2 Akorinto 10:11
6 Mawu Ofanana  

Pakuti, makalatatu, ati, ndiwo olemera, ndi amphamvu; koma maonekedwe a thupi lake ngofooka, ndi mau ake ngachabe.


Pakuti sitilimba mtima kudziwerenga, kapena kudzilinganiza tokha ndi ena a iwo amene adzivomeretsa okha; koma iwowa, podziyesera okha ndi iwo okha, ndi kudzilinganiza okha ndi iwo okha, alibe nzeru.


Pakuti ndiopa, kuti kaya, pakudza ine, sindidzakupezani inu otere onga ndifuna, ndipo ine ndidzapezedwa ndi inu wotere wonga simufuna; kuti kaya pangakhale chotetana, kaduka, mikwiyo, zilekanitso, maugogodi, ukazitape, zodzikuza, mapokoso;


Chifukwa cha ichi ndilembera izi pokhala palibe ine, kuti pokhala ndili pomwepo ndingachite mowawitsa, monga mwa ulamuliro umene Ambuye anandipatsa ine wakumangirira, ndipo si wakugwetsa.