Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 17:9 - Buku Lopatulika

Akakhoza iyeyo kuponyana ndi ine ndi kundipha, tidzakhala ife akapolo anu; koma ine ndikamgonjetsa ndi kumupha, tsono mudzakhala inu akapolo athu, ndi kutitumikira ife.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Akakhoza iyeyo kuponyana ndi ine ndi kundipha, tidzakhala ife akapolo anu; koma ine ndikamlaka, ndi kumupha, tsono mudzakhala inu akapolo athu, ndi kutitumikira ife.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngati angathe kulimbana nane ndi kundipha, ndiye kuti Afilisti tonse tidzakhala akapolo anu. Koma ndikampambana ndi kumupha, inuyo mudzakhala akapolo athu ndi kumatigwirira ntchito.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngati angathe kumenyana nane ndi kundipha, ife tidzakhala akapolo anu, koma ngati ine ndimugonjetsa ndi kumupha, inu mudzakhala akapolo athu ndi kumatitumikira.”

Onani mutuwo



1 Samueli 17:9
3 Mawu Ofanana  

Ndipo Abinere mwana wa Nere ndi anyamata a Isiboseti mwana wa Saulo anatuluka ku Mahanaimu kunka ku Gibiyoni.


Pamenepo Nahasi Mwamoni anakwera, namanga Yabesi-Giliyadi zithando; ndipo anthu onse a ku Yabesi anati kwa Nahasi, Mupangane chipangano ndi ife, ndipo tidzakutumikirani inu.


Nati Mfilistiyo, Ine ndinyoza makamu a nkhondo a Israele lero; mundipatse munthu, kuti tilimbane ife awiri.