Koma Aminoni anali ndi bwenzi lake, dzina lake ndiye Yonadabu, mwana wa Simea, mbale wa Davide. Ndipo Yonadabu anali munthu wochenjera ndithu.
1 Samueli 16:9 - Buku Lopatulika Pamenepo Yese anapititsapo Sama. Ndipo anati, Koma uyunso Yehova sanamsankhe. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Pamenepo Yese anapititsapo Sama. Ndipo anati, Koma uyunso Yehova sanamsankhe. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Pamenepo Yese adaitana Sama kuti apite kwa Samuele. Koma Samuele adati, “Ameneyunso Chauta sadamsankhe.” Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Ndipo Yese anayitana Sama, koma Samueli anati, “Ngakhale uyu Yehova sanamusankhe.” |
Koma Aminoni anali ndi bwenzi lake, dzina lake ndiye Yonadabu, mwana wa Simea, mbale wa Davide. Ndipo Yonadabu anali munthu wochenjera ndithu.
ndi Yese anabala mwana wake wamwamuna woyamba Eliyabu, ndi Abinadabu wachiwiri, ndi Simea wachitatu,
Ndipo Yese anapititsapo ana ake aamuna asanu ndi awiri. Koma Samuele anati kwa Yese, Yehova sanawasankhe awa.
Ndipo ana atatu aakulu a Yese anatsata Saulo kunkhondoko; ndi maina ao a ana ake atatuwo adapita ku nkhondowo ndiwo Eliyabu woyambayo, ndi mnzake womponda pamutu pake Abinadabu, ndi wachitatu Sama.