Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Zekariya 7:7 - Buku Lopatulika

7 Si ndiwo mau Yehova anawalalikira mwa aneneri oyamba aja, muja Yerusalemu anali nao okhalamo, ndi wokhazikika; ndi m'mizinda mwake pozungulira pake, ndi m'dziko la kumwera, ndi m'chidikha munali anthu okhalamo?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

7 Si ndiwo mau Yehova anawalalikira mwa aneneri oyamba aja, muja Yerusalemu anali nao okhalamo, ndi wokhazikika; ndi m'midzi mwake pozungulira pake, ndi m'dziko la kumwera, ndi m'chidikha munali anthu okhalamo?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

7 Pajatu nzimenezi zija ankanena Chautazi kudzera mwa aneneri akale, pamene munali modzaza ndi anthu ndiponso zinthu zinkapita m'tsogolo mu mzinda wa Yerusalemu ndi m'mizinda yake yozungulira, ku madera a kumwera ndi ku chigwa.’ ”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’ ”

Onani mutuwo Koperani




Zekariya 7:7
23 Mawu Ofanana  

Tcherani khutu lanu, mudze kwa Ine, imvani, mzimu wanu nudzakhala ndi moyo; ndipo ndidzapangana nanu chipangano chosatha, ndicho zifundo zoona za Davide.


Mizinda ya kumwera yatsekedwa, palibe wotsegulira. Yuda yense wachotsedwa m'ndende yenseyo, wachotsedwa m'nsinga.


Ndipo adzachokera kumizinda ya Yuda, ndi kumalo akuzungulira Yerusalemu, ndi kudziko la Benjamini, ndi kuchidikha, ndi kumapiri, ndi kumwera, ndi kudza nazo nsembe zopsereza, ndi nsembe zophera, ndi nsembe zaufa, ndi lubani, ndi kudza nazo zamayamikiro, kunyumba ya Yehova.


Ndinanena ndi iwe m'phindu lako; koma unati, Sindidzamva. Awa ndi makhalidwe ako kuyambira ubwana wako, kuti sudamvere mau anga.


Anthu adzagula minda ndi ndalama, adzalembera makalata ogulira, adzawasindikiza, adzaitana mboni, m'dziko la Benjamini, ndi m'malo ozungulira Yerusalemu, ndi m'mizinda ya Yuda, ndi m'mizinda ya kumtunda, ndi m'mizinda ya kuchidikha, ndi m'mizinda ya kumwera; pakuti ndidzabweza undende wao, ati Yehova.


M'mizinda ya kumtunda, m'mizinda ya kuchidikha, m'mizinda ya kumwera, m'dziko la Benjamini, m'malo ozungulira Yerusalemu, m'mizinda ya Yuda, zoweta zidzapitanso pansi pa manja a iye amene aziwerenga, ati Yehova.


Koma ndinatuma kwa inu atumiki anga onse aneneri, ndinauka mamawa ndi kuwatuma, ndi kuti, Musachitetu chonyansa ichi ndidana nacho.


koma chinthu ichi ndinawauza, kuti, Mverani mau anga, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu, ndipo inu mudzakhala anthu anga; nimuyende m'njira yonse imene ndakuuzani inu, kuti chikukomereni.


Pakuti mukakonzatu njira zanu ndi machitidwe anu; ndi kuweruzatu milandu ya munthu ndi mnansi wake;


Inde, anasanduliza mitima yao ikhale ngati mwala woti gwaa, kuti angamve chilamulo, ndi mau amene Yehova wa makamu anatumiza ndi Mzimu wake mwa aneneri oyamba aja; m'menemo munafuma mkwiyo waukulu wochokera kwa Yehova wa makamu.


Ndipo pamene mukadya si ndinu, mukamwa si ndinu kodi?


Ndipo mau a Yehova anadza kwa Zekariya, ndi kuti,


ndi kumwera, ndi chidikha cha chigwa cha Yeriko, mzinda wa migwalangwa, kufikira ku Zowari.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa