Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 14:4 - Buku Lopatulika

4 Ndipo kumene ndinkako Ine, mudziwa njira yake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

4 Ndipo kumene ndinkako Ine, mudziwa njira yake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

4 Ndipo kumene ndikupita Ineko, njira yake mukuidziŵa.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

4 Inu mukudziwa njira ya kumene Ine ndikupita.”

Onani mutuwo Koperani




Yohane 14:4
13 Mawu Ofanana  

Kodi sanayenere Khristu kumva zowawa izi, ndi kulowa ulemerero wake?


Ine ndine khomo; ngati wina alowa ndi Ine, adzapulumutsidwa, nadzalowa, nadzatuluka, nadzapeza busa.


Ngati wina anditumikira Ine, anditsate; ndipo kumene kuli Ine, komwekonso kudzakhala mtumiki wanga. Ngati wina anditumikira Ine, Atate adzamchitira ulemu iyeyu.


Yesu, podziwa kuti Atate adampatsa Iye zonse m'manja mwake, ndi kuti anachokera kwa Mulungu, namuka kwa Mulungu,


M'nyumba ya Atate wanga alimo malo okhalamo ambiri. Ngati sikudali kutero, ndikadakuuzani inu; pakuti ndipita kukukonzerani inu malo.


Mwamva kuti Ine ndinanena kwa inu, Ndimuka, ndipo ndidza kwa inu. Mukadandikonda Ine, mukadakondwera kuti ndipita kwa Atate; pakuti Atate ali wamkulu ndi Ine.


Ndipo ngati ndipita kukakonzera inu malo, ndidzabweranso, ndipo ndidzalandira inu kwa Ine ndekha; kuti kumene kuli Ineko, mukakhale inunso.


Tomasi ananena ndi Iye, Ambuye, sitidziwa kumene munkako; tidziwa njira bwanji?


Ndinatuluka mwa Atate, ndipo ndadza kudziko lapansi: ndilisiyanso dziko lapansi, ndipo ndipita kwa Atate.


Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.


Pakuti chifuniro cha Atate wanga ndi ichi, kuti yense wakuyang'ana Mwana, ndi kukhulupirira Iye, akhale nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa