Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 11:53 - Buku Lopatulika

53 Chifukwa chake, kuyambira tsiku lomwelo anapangana kuti amuphe Iye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

53 Chifukwa chake, kuyambira tsiku lomwelo anapangana kuti amuphe Iye.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

53 Kuyambira tsiku limenelo akulu aja a Ayuda adayamba kupangana zoti amuphe.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

53 Choncho kuyambira tsiku limeneli iwo anakonzekera za kuti amuphe.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 11:53
22 Mawu Ofanana  

Ndipo iwo anamuona iye ali patali, ndipo asanayandikire pafupi ndi iwo, anampangira iye chiwembu kuti amuphe.


Koma ndinawachitira umboni wakuwatsutsa, ndinanena nao, Mugoneranji pafupi pa linga? Mukateronso ndikuthirani manja. Kuyambira pomwepo sanafikenso pa Sabata.


Ndipo kuyambira pamenepo gawo lina la anyamata anga anagwira ntchito, ndi gawo lina linagwira nthungo, zikopa, ndi mauta, ndi malaya achitsulo; ndi akulu anali m'mbuyo mwa nyumba yonse ya Yuda.


Lodala dzina la Yehova Kuyambira tsopano kufikira kosatha.


Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,


Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri, mantha andizinga. Pondipangira chiwembu, anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.


Pakuti adani anga alankhula za ine; ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,


Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Ndikakufotokozerani, kodi simudzandipha ine? Ndipo ndikakupangirani, simudzandimvera ine.


Ndipo akulu anati kwa mfumu, Munthu uyu aphedwetu; chifukwa analopetsa manja a anthu a nkhondo otsala m'mzinda muno, ndi manja a anthu onse, pakunena kwa iwo mau otero; pakuti munthu uyu safuna mtendere wa anthu awa, koma nsautso yao.


Ndipo Afarisi anatuluka, nakhala upo womchitira Iye mwa kumuononga.


Kuyambira pamenepo Yesu anayamba kuwalangiza ophunzira ake, kuti kuyenera Iye amuke ku Yerusalemu, kukazunzidwa zambiri ndi akulu, ndi ansembe aakulu, ndi alembi; ndi kukaphedwa, ndi tsiku lachitatu kuuka kwa akufa.


Ndipo sanalimbike mtima munthu aliyense kumfunsa kanthu kuyambira tsiku lomwelo.


nakhala upo wakuti amgwire Yesu ndi chinyengo, namuphe.


Ndipo ansembe aakulu ndi akulu a milandu onse anafunafuna umboni wonama wakutsutsa Yesu, kuti amuphe Iye;


Ndipo popita masiku awiri kuli phwando la Paska ndi Mkate wopanda chotupitsa; ndipo ansembe aakulu ndi alembi anafunafuna momchitira chiwembu, ndi kumupha:


Ndipo Afarisi anatuluka, ndipo pomwepo anamkhalira upo ndi Aherode, wakumuononga Iye.


Pamenepo ansembe aakulu ndi Afarisi anasonkhanitsa akulu, nanena, Titani ife? Chifukwa munthu uyu achita zizindikiro zambiri.


Koma ansembe aakulu anapangana kuti akaphe Lazaronso;


Ndipo zitapita izi Yesu anayendayenda mu Galileya; pakuti sanafune kuyendayenda mu Yudeya, chifukwa Ayuda anafuna kumupha Iye.


Koma m'mene anamva iwo analaswa mtima, nafuna kuwapha.


Ndipo atapita masiku ambiri, Ayuda anapangana kuti amuphe iye;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa