Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 11:24 - Buku Lopatulika

24 Marita ananena ndi Iye, Ndidziwa kuti adzauka m'kuuka tsiku lomaliza.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

24 Marita ananena ndi Iye, Ndidziwa kuti adzauka m'kuuka tsiku lomaliza.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

24 Marita adati, “Ndikudziŵa kuti adzauka podzauka anthu kwa akufa pa tsiku lomaliza.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

24 Marita anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti adzauka pa kuukanso pa tsiku lomaliza.”

Onani mutuwo Koperani




Yohane 11:24
18 Mawu Ofanana  

Koma ine ndidzapenyerera nkhope yanu m'chilungamo, ndidzakhuta mtima ndi maonekedwe anu, pamene ndidzauka.


Iye wameza imfa kunthawi yonse; ndipo Ambuye Mulungu adzapukuta misozi pa nkhope zonse; ndipo chitonzo cha anthu ake adzachichotsa padziko lonse lapansi; chifukwa Yehova wanena.


Akufa anu adzakhala ndi moyo; mitembo yao idzauka. Ukani muimbe, inu amene mukhala m'fumbi; chifukwa mame ako akunga mame a pamasamba, ndipo dziko lapansi lidzatulutsa mizimu.


Ndidzawaombola kumphamvu ya kumanda, ndidzawaombola kuimfa; imfa, miliri yako ili kuti? Kulekerera kudzabisika pamaso panga.


Atapita masiku awiri adzatitsitsimutsa, tsiku lachitatu adzatiutsa; ndipo tidzakhala ndi moyo pamaso pake.


ndipo udzakhala wodala; chifukwa iwo alibe chakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa olungama.


Yesu ananena naye, Mlongo wako adzauka.


Koma chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi ichi, kuti za ichi chonse Iye anandipatsa Ine ndisatayeko kanthu, koma ndichiukitse tsiku lomaliza.


Pakuti chifuniro cha Atate wanga ndi ichi, kuti yense wakuyang'ana Mwana, ndi kukhulupirira Iye, akhale nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomaliza.


ndi kukhala nacho chiyembekezo cha kwa Mulungu chimene iwo okhanso achilandira, kuti kudzakhala kuuka kwa olungama ndi osalungama.


Akazi analandira akufa ao mwa kuuka kwa akufa; ndipo ena anakwapulidwa, osalola kuomboledwa,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa