Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yohane 1:11 - Buku Lopatulika

11 Anadza kwa zake za Iye yekha, ndipo ake a mwini yekha sanamlandire Iye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Anadza kwa zake za Iye yekha, ndipo ake a mwini yekha sanamlandire Iye.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Adaabwera kwao ndithu, koma anthu ake omwe sadamlandire.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.

Onani mutuwo Koperani




Yohane 1:11
17 Mawu Ofanana  

Ndipo Iye anayankha, nati, Sindinatumidwa kwa ena koma kwa nkhosa zotayika za banja la Israele.


Koma mfulu za pamudzi pake zinamuda, nkutuma akazembe amtsate m'mbuyo ndi kunena, Ife sitifuna munthuyo akhale mfumu yathu.


Anali m'dziko lapansi, ndi dziko linalengedwa ndi Iye, koma dziko silinamzindikira Iye.


Koma onse amene anamlandira Iye, kwa iwo anapatsa mphamvu yakukhala ana a Mulungu, kwa iwotu, akukhulupirira dzina lake;


Pamene ananena kwa wophunzirayo, Taona, amai wako. Ndipo kuyambira ora lomweli wophunzirayo ananka naye kwao.


Chimene anachiona nachimva, achita umboni wa ichi chomwe; ndipo kulibe munthu alandira umboni wake.


Amuna, abale, ana a mbadwa ya Abrahamu, ndi iwo mwa inu akuopa Mulungu, kwa ife atumidwa mau a chipulumutso ichi.


Ndipo Paulo ndi Barnabasi analimbika mtima ponena, nati, Kunafunika kuti mau a Mulungu ayambe alankhulidwe kwa inu. Popeza muwakankha, nimudziyesera nokha osayenera moyo wosatha, taonani, titembenukira kwa amitundu.


ndi kulawirana; ndipo tinalowa m'ngalawa, koma iwo anabwera kwao.


Ndipo ndinena kuti Khristu anakhala mtumiki wa mdulidwe, chifukwa cha choonadi cha Mulungu, kuti alimbikitse malonjezo opatsidwa kwa makolo,


Ndinena zoona mwa Khristu, sindinama ai, chikumbumtima changa chichita umboni pamodzi ndine mwa Mzimu Woyera,


a iwo ali makolo, ndi kwa iwo anachokera Khristu, monga mwa thupi, ndiye Mulungu wa pamwamba pa zonse wolemekezeka kunthawi zonse. Amen.


koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wake, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa