Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Yeremiya 10:8 - Buku Lopatulika

8 Koma onse pamodzi apulukira ndi kupusa; mtengo ndiwo chilangizo, chopanda pake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

8 Koma onse pamodzi apulukira ndi kupusa; mtengo ndiwo chilangizo, chopanda pake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru. Nzeru zao amaphunzira ku mafano achabechabe opanga ndi mitengo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

8 Onsewo ndi opusa ndi opanda nzeru; malangizo awo amawatenga kuchokera kwa mafano achabechabe opanga ndi mitengo.

Onani mutuwo Koperani




Yeremiya 10:8
16 Mawu Ofanana  

Adzafanana nao iwo akuwapanga; ndi onse akuwakhulupirira.


Akuwapanga adzafanana nao; inde, onse akuwakhulupirira.


Taona, iwo onse, ntchito zao zikhala zopanda pake ndi zachabe; mafano ao osungunula ndiwo mphepo ndi masokonezo.


Iwo sadziwa, kapena kuzindikira, chifukwa pamaso mwao papakidwa thope, kuti sangaone, ndi m'mitima mwako kuti sangadziwitse.


Palibe wina wokumbukira, kapena kudziwa, kapena kuzindikira, ndi kuti, Ndatentha mbali ina pamoto, inde ndaotchanso mkate pamakala pake, ndakazinga nyama ndi kuidya; kodi ndichipange chotsala chake, chikhale chonyansa? Ndidzagwadira kodi tsinde la mtengo?


Anthu onse ali opulukira ndi opanda nzeru; woyenga yense anyazitsidwa ndi fanizo lake losemasema; pakuti fanizo lake loyenga lili bodza, mulibe mpweya mwa iwo.


amene ati kwa mtengo, Iwe ndiwe atate wanga; ndi kwa mwala, Wandibala; pakuti anandipatsa Ine mbuyo, si nkhope yao; koma m'nthawi ya kuvutidwa kwao adzati, Ukani, tipulumutseni.


Ndipo kunali kuti mbiri ya dama lake inaipitsa dziko, ndipo anachita chigololo ndi miyala ndi mitengo.


Pakuti anthu anga apusa, sandidziwa Ine; ali ana opulukira sazindikira; ali ochenjera kuchita choipa koma kuchita chabwino sakudziwa.


Ndipo ine ndinati, Ndithu amenewo ali aumphawi; ali opusa; pakuti sadziwa njira ya Yehova, kapena chiweruzo cha Mulungu wao.


Anthu anga afunsira kumtengo wao, ndi ndodo yao iwafotokozera; pakuti mzimu wachigololo wawalakwitsa, ndipo achita chigololo kuchokera Mulungu wao.


Iwo osamalira mabodza opanda pake ataya chifundo chaochao.


Apindulanji nalo fano losema, kuti wakulipanga analisema; fano loyenga ndi mphunzitsi wamabodza, kuti wakulipanga alikhulupirira, atapanga mafano osanena mau?


Pakuti aterafi anena zopanda pake, ndi aula aona bodza; nafotokoza maloto achabe, asangalatsa nazo zopanda pake; chifukwa chake ayendayenda ngati nkhosa, azunzika popeza palibe mbusa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa