Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 19:15 - Buku Lopatulika

15 Ndi zotengera zonse zovundukuka, zopanda chivundikiro chomangikapo, zili zodetsedwa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

15 Ndi zotengera zonse zovundukuka, zopanda chivundikiro chomangikapo, zili zodetsedwa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

15 Ndipo chiŵiya chilichonse chopanda chivundikiro nchoipitsidwa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

15 ndiponso chiwiya chilichonse chopanda chivundikiro chidzakhala chodetsedwa.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 19:15
6 Mawu Ofanana  

Ndipo chilichonse chakufa cha izi chikagwera kanthu, kanthuka kadzakhala kodetsedwa; ngakhale chipangizo chamtengo, kapena chovala, kapena chikopa kapena thumba, chipangizo chilichonse chimene agwira nacho ntchito, achiviike m'madzi, ndipo chidzakhala chodetsedwa kufikira madzulo; pamenepo chidzakhala choyera.


Ndipo chilichonse cha izi chikagwa m'chotengera chilichonse chadothi, chinthu chokhala m'mwemo chidetsedwa, ndi chotengeracho muchiswe.


Ndipo wansembe aziuza kuti atulutse zonse za m'nyumba, asanalowe kudzaona nthendayi, zinthu zonse zili m'nyumba zingakhale zodetsedwa; ndipo atatero wansembe alowe kukaona nyumbayi;


Chilamulo ndi ichi: Munthu akafa m'hema, yense wakulowa m'hemamo, ndi yense wakukhala m'hemamo, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri.


Ndipo aliyense wakukhudza munthu wophedwa ndi lupanga, kapena mtembo, kapena fupa la munthu, kapena manda, pathengo poyera, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri.


Muyeretse zovala zanu zonse, zipangizo zonse zachikopa, ndi zoomba zonse za ubweya wa mbuzi, ndi zipangizo zonse za mtengo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa