Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Numeri 15:21 - Buku Lopatulika

21 Muzipatsa Yehova nsembe yokweza yoitenga ku mtanda wanu woyamba, mwa mibadwo yanu.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

21 Muzipatsa Yehova nsembe yokweza yoitenga ku mtanda wanu woyamba, mwa mibadwo yanu.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

21 Muzidzapereka motero kwa Chauta buledi mmodzi mwa buledi wanu woyamba pa mibadwo yanu yonse.’

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

21 Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.

Onani mutuwo Koperani




Numeri 15:21
8 Mawu Ofanana  

Ndipo wansembe mwana wa Aroni azikhala ndi Alevi, polandira Alevi limodzilimodzi la magawo khumi; ndi Alevi azikwera nalo limodzi la magawo khumi mwa limodzilimodzi la magawo khumi kunyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda, kunyumba ya chuma.


Uzibwera nazo zoyambayamba za m'munda mwako kunyumba ya Yehova Mulungu wako. Usaphike mwanawambuzi mu mkaka wa make.


ndipo zikhale za Aroni ndi za ana ake aamuna, mwa lemba losatha, ziwadzere kwa ana a Israele; popeza ndiyo nsembe yokweza; ndipo ikhale nsembe yokweza yodzera kwa ana a Israele, ya kwa nsembe zamtendere zao, ndiyo nsembe yao yokweza ya Yehova.


Ndi zoyamba za zipatso zoyamba za zinthu zilizonse, ndi nsembe zokweza zilizonse za nsembe zanu zonse zokweza nza ansembe; muperekenso ufa wanu woyamba kwa wansembe, kuti mdalitso ukhalebe pa nyumba yako.


Musamadya mkate, kapena tirigu wokazinga, kapena ngala zaziwisi, kufikira tsiku lomweli, kufikira mutadza nacho chopereka cha Mulungu wanu; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu m'nyumba zanu zonse.


Pa mtanda wanu woyamba muperekeko kamtanda, kakhale nsembe yokweza; monga mumachitira nsembe yokweza ya popuntha tirigu, momwemo muzikakweza,


Ndipo pamene mulakwa, osachita mau awa onse amene Yehova ananena ndi Mose;


Unenenso ndi Alevi, nuti nao, Pamene mulandira kwa ana a Israele, limodzi la magawo khumi limene ndakupatsani likhale cholowa chanu chochokera kwao, muziperekako nsembe yokweza ya Yehova, limodzi la magawo khumi la limodzi la magawo khumi.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa