Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Nehemiya 5:6 - Buku Lopatulika

6 Ndipo pakumva kulira kwao, ndi mau ao, kunandiipira kwambiri.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 Ndipo pakumva kulira kwao, ndi mau ao, kunandiipira kwambiri.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Ine nditamva madandaulo amenewo, ndidapsa mtima kwambiri.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.

Onani mutuwo Koperani




Nehemiya 5:6
8 Mawu Ofanana  

Ndipo ndinatsutsana nao, ndi kuwatemberera, ndi kukantha ena a iwo, ndi kumwetula tsitsi lao, ndi kuwalumbiritsa pa Mulungu ndi kuti, Musapereke ana anu aakazi kwa ana ao aamuna, kapena kutengera ana anu aamuna, kapena a inu nokha, ana ao aakazi.


Ndipo ndinaipidwa nacho kwambiri, motero ndinataya kubwalo akatundu onse a m'nyumba ya Tobiya, kuwachotsa m'chipindamo.


Pamenepo mtima wanga unandipangira; ndipo ndinatsutsana nao aufulu ndi olamulira, ndi kunena nao, Mukongoletsa mwa phindu yense kwa mbale wake. Ndipo ndinasonkhanitsa msonkhano waukulu wakuwatsutsa.


Ndinasumwa kwakukulu, chifukwa cha oipa akusiya chilamulo chanu.


Ndipo anyamata ako onse awa adzanditsikira, nadzandigwadira, ndi kuti, Tulukani inu, ndi anthu onse akukutsatani; ndipo pambuyo pake ndidzatuluka. Ndipo anatuluka kwa Farao wakupsa mtima.


Pamenepo Mose adapsa mtima, ndipo anati kwa Yehova, Musasamalira chopereka chao; sindinalande bulu wao mmodzi, kapena kuchitira choipa mmodzi wa iwowa.


Ndipo m'mene anawaunguza ndi mkwiyo, ndi kumva chisoni chifukwa cha kuuma kwa mitima yao, ananena kwa munthuyo, Tambasula dzanja lako. Ndipo analitambasula; ndipo linachira dzanja lake.


Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa