Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Nehemiya 13:10 - Buku Lopatulika

10 Ndinazindikiranso kuti sanapereke kwa Alevi magawo ao; m'mwemo Alevi ndi oimbira adathawira yense kumunda wake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

10 Ndinazindikiranso kuti sanapereke kwa Alevi magawo ao; m'mwemo Alevi ndi oimbira adathawira yense kumunda wake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

10 Ndidapezanso kuti Alevi sankaŵapatsa magawo ao amene ankayenera kulandira. Choncho Aleviwo, pamodzi ndi anthu oimba nyimbo amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, adathaŵa, aliyense kupita ku munda wake.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

10 Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.

Onani mutuwo Koperani




Nehemiya 13:10
11 Mawu Ofanana  

Anauzanso anthu okhala mu Yerusalemu apereke gawo la ansembe ndi Alevi, kuti iwowa alimbike m'chilamulo cha Yehova.


ndi kuti tidzabwera nazo za mtanda wa mkate wathu woyamba, ndi nsembe zathu zokwera, ndi zipatso za mtengo uliwonse, vinyo, ndi mafuta, kwa ansembe, kuzipinda za nyumba ya Mulungu wathu; ndi limodzi la magawo khumi la nthaka yathu kwa Alevi; pakuti Alevi amene amalandira limodzilimodzi la magawo khumi m'midzi yonse yolima ife.


Pakuti ana a Israele ndi ana a Levi, azibwera nayo nsembe yokweza yatirigu, ndi yavinyo ndi yamafuta, kuzipinda kuli zipangizo za malo opatulika, ndi ansembe akutumikira, ndi odikira, ndi oimbira; kuti tisasiye nyumba ya Mulungu wathu.


Ndi Aisraele onse m'masiku a Zerubabele, ndi m'masiku a Nehemiya, anapereka magawo a oimbira ndi odikira, monga mudafunika tsiku ndi tsiku; nawapatulira Alevi; ndi Alevi anawapatulira ana a Aroni.


Iwe sunanditengere Ine zoweta zazing'ono za nsembe zopsereza zako; kapena kundilemekeza ndi nsembe zako. Sindinakutumikiritse ndi nsembe zaufa, kapena kukutopetsa ndi lubani.


Kodi munthu adzalanda za Mulungu? Ndipo inu mundilanda Ine. Koma mukuti, Takulandani zotani? Limodzilimodzi la magawo khumi, ndi zopereka.


Uza ana a Israele, kuti apatseko Alevi cholowa chaochao, mizinda yokhalamo; muwapatsenso Alevi mabusa akuzungulira mizinda.


Dzichenjerani nokha, musataye Mlevi masiku onse akukhala inu m'dziko mwanu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa