Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mlaliki 2:6 - Buku Lopatulika

6 ndinadzipangira ndekha matamanda a madzi akuthirira madzi m'nkhalango momeramo mitengo;

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

6 ndinadzipangira ndekha matamanda a madzi akuthirira madzi m'nkhalango momeramo mitengo;

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

6 Ndidaakumbanso maiŵe oti madzi ake azithirira minda ya mitengo yobzala ija.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

6 Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija.

Onani mutuwo Koperani




Mlaliki 2:6
7 Mawu Ofanana  

Ndipo ndinapitirira kunka ku Chipata cha Chitsime, ndi ku Dziwe la Mfumu; koma popita nyama ili pansi panga panaichepera.


ndi kalata kwa Asafu wosunga misitu ya mfumu, kuti andipatse mitengo ya mitanda ya kuzipata za linga lili ku Kachisi, ndi ya linga la mzinda, ndi ya nyumba imene ndidzalowamo ine. Ndipo mfumu inandipatsa monga mwa dzanja lokoma la Mulungu londikhalira.


Ndi Chipata cha ku Kasupe anachikonza Salumu mwana wa Kolihoze mkulu wa dziko la Mizipa anachimanga, nachikomaniza pamwamba pake, naika zitseko zake, zokowera zake, ndi mipiringidzo yake; ndiponso linga la dziwe la Sela pamunda wa mfumu, ndi kufikira kumakwerero otsikira kumzinda wa Davide.


Potsatizana naye anakonza Nehemiya mwana wa Azibuki, mkulu wa dera lake lina la dziko la Betezuri, mpaka malo a pandunji pa manda a Davide, ndi ku dziwe adalikumba, ndi kunyumba ya amphamvu aja.


Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi; wakupatsa chipatso chake pa nyengo yake, tsamba lake lomwe losafota; ndipo zonse azichita apindula nazo.


Khosi lako likunga nsanja yaminyanga; maso ako akunga matawale a ku Hesiboni, a pa chipata cha Batirabimu; mphuno yako ikunga nsanja ya ku Lebanoni imene iloza ku Damasiko.


Ndipo adzakhala ngati mtengo wooka kuli madzi, wotambalitsa mizu yake pamtsinje, wosaopa pofika nyengo yadzuwa, koma tsamba lake likhala laliwisi; ndipo suvutika chaka cha chilala, suleka kubala zipatso.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa