Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 26:54 - Buku Lopatulika

54 Koma pakutero malembo adzakwaniridwa bwanji, pakuti kuyenera chomwecho?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

54 Koma pakutero malembo adzakwaniridwa bwanji, pakuti kuyenera chomwecho?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

54 Koma ndikadatero, nanga zikadachitika bwanji zimene Malembo adaneneratu kuti ziyenera kuchitika?”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

54 Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 26:54
11 Mawu Ofanana  

Galamuka, lupanga, pa mbusa wanga, ndi pa munthu mnzanga wa pamtima, ati Yehova wa makamu; kantha mbusa, ndi nkhosa zidzabalalika; koma ndidzabwezera dzanja langa pa zazing'onozo.


Yesu ananena kwa iwo, Kodi simunawerenge konse m'malembo, Mwala umene anaukana omanga nyumba womwewu unakhala mutu wa pangodya: Ichi chinachokera kwa Ambuye, ndipo chili chozizwitsa m'maso mwathu?


Mwana wa Munthu achokatu, monga kunalembedwa za Iye; koma tsoka ali nalo munthu amene Mwana wa Munthu aperekedwa ndi iye! Kukadakhala bwino kwa munthuyo ngati sakadabadwa.


Ngati anawatcha milungu iwo amene mau a Mulungu anawadzera (ndipo cholemba sichingathe kuthyoka),


Amuna inu, abale, kunayenera kuti lemba likwanitsidwe, limene Mzimu Woyera anayamba kunena mwa m'kamwa mwa Davide za Yudasi, wokhala mtsogoleri wa iwo adagwira Yesu.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa