Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 26:46 - Buku Lopatulika

46 Ukani, timuke; taonani, iye wakundipereka wayandikira.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

46 Ukani, timuke; taonani, iye wakundipereka wayandikira.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

46 Dzukani, tiyeni tizipita. Suuyu wodzandipereka uja, wafika.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

46 Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 26:46
11 Mawu Ofanana  

Pomwepo anadza kwa ophunzira, nanena kwa iwo, Gonani nthawi yatsalayi, mupumule; onani, nthawi yafika, ndipo Mwana wa Munthu aperekedwa m'manja a ochimwa.


Ndipo Iye ali chilankhulire, onani, Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anadza, ndi pamodzi ndi iye khamu lalikulu la anthu, ndi malupanga ndi mikunkhu, kuchokera kwa ansembe aakulu ndi akulu a anthu.


Ukani, tizimuka; onani wakundiperekayo ali pafupi.


Koma ndili ndi ubatizo ndikabatizidwe nao; ndipo ndikanikizidwa Ine kufikira ukatsirizidwa!


Ndipo anati kwa iwo, Ndinalakalaka ndithu kudya Paska uwu pamodzi ndinu, ndisanayambe kusautsidwa;


Koma onani, dzanja lake la iye amene adzandipereka ali pagome pano pamodzi ndi Ine.


Ndipo panali, pamene anayamba kukwanira masiku akuti alandiridwe Iye kumwamba, Yesu anatsimikiza kuloza nkhope yake kunka ku Yerusalemu,


koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti ndikonda Atate, ndi kuti ndichita monga momwe Atate wandilamula. Nyamukani, tizimuka kuchokera kuno.


Petro, m'mene anacheuka, anapenya wophunzira amene Yesu anamkonda alikutsata, amenenso anatsamira pachifuwa pake pamgonero, nati, Ambuye, ndani iye wakupereka Inu?


Pamenepo Paulo anayankha, Muchitanji, polira ndi kundiswera mtima? Pakuti ndakonzeka ine si kumangidwa kokha, komatunso kufera ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.


Ndipo kunali, pamene Mfilistiyo anadzikonza, nadza, nasendera pafupi kuti akomane ndi Davide, Davide anafulumira, nathamangira ku khamulo, kuti akomane ndi Mfilistiyo.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa