Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Mateyu 26:27 - Buku Lopatulika

27 Ndipo pamene anatenga chikho, anayamika, napatsa iwo, nanena, Mumwere ichi inu nonse,

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

27 Ndipo pamene anatenga chikho, anayamika, napatsa iwo, nanena, Mumwere ichi inu nonse,

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

27 Kenaka adatenga chikho, nathokoza Mulungu nkuchipereka kwa ophunzirawo. Adaŵauza kuti, “Imwani nonsenu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

27 Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.

Onani mutuwo Koperani




Mateyu 26:27
12 Mawu Ofanana  

Ndidzanyamula chikho cha chipulumutso, ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.


Ndalowa m'munda mwanga, mlongo wanga, mkwatibwi: Ndatchera mure wanga ndi zonunkhiritsa zanga; ndadya uchi wanga ndi chisa chake; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Idyani, atsamwalinu, imwani, mwetsani chikondi.


M'kamwa mwako munge ngati vinyo woposa, womeza tseketseke bwenzi langa, wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.


Ndipo m'phiri limeneli Yehova wa makamu adzakonzera anthu ake onse phwando la zinthu zonona, phwando la vinyo wa pamitsokwe, la zinthu zonona za mafuta okhaokha, la vinyo wansenga wokuntha bwino.


Inu nonse, inu akumva ludzu, idzani kumadzi; ndi osowa ndalama idzani inu mugule mudye; inde idzani, mugule vinyo ndi mkaka opanda ndalama ndi opanda mtengo wake.


natenga mikateyo isanu ndi iwiri ndi nsombazo; nayamika Mulungu, nanyema, napatsa kwa ophunzira, ndi ophunzira kwa anthu.


Ndipo pamene iwo analinkudya, Yesu anatenga mkate, nadalitsa, naunyema; ndipo m'mene anapatsa kwa ophunzira, anati, Tengani, idyani; ichi ndi thupi langa.


pakuti ichi ndi mwazi wanga wa pangano wothiridwa chifukwa cha anthu ambiri ku kuchotsa machimo.


Ndipo choteronso chikho, atatha mgonero, nanena, Chikho ichi ndi pangano latsopano m'mwazi wanga wothiridwa chifukwa cha inu.


Chikho cha dalitso chimene tidalitsa, sichili chiyanjano cha mwazi wa Khristu kodi? Mkate umene tinyema suli chiyanjano cha thupi la Khristu kodi?


Koma munthu adziyese yekha, ndi kotero adye mkate, ndi kumwera chikho.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa