Maliro 1:1 - Buku Lopatulika1 Ha! Mzindawo unadzala anthu, ukhalatu pa wokha! Ukunga mkazi wamasiye! Waukuluwo mwa amitundu, kalonga wamkazi m'madera a dziko wasanduka wolamba! Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20141 Ha! Mudziwo unadzala anthu, ukhalatu pa wokha! Ukunga mkazi wamasiye! Waukuluwo mwa amitundu, kalonga wamkazi m'madera a dziko wasanduka wolamba! Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa1 Ha! Mzinda wa Yerusalemu wakhala wokhawokha, m'menemo kale udaali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu, koma tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mzinda wolemekezeka koposa mizinda ina, koma tsopano wasanduka kapolo. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero1 Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo. Onani mutuwo |