Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 6:2 - Buku Lopatulika

2 Koma Afarisi ena anati, Muchitiranji chosaloledwa kuchitika tsiku la Sabata?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

2 Koma Afarisi ena anati, Muchitiranji chosaloledwa kuchitika tsiku la Sabata?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

2 Apo Afarisi ena adafunsa kuti, “Bwanji mukuchita zimene siziloledwa pa tsiku la Sabata?”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Ena mwa Afarisi anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mukuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata?”

Onani mutuwo Koperani




Luka 6:2
14 Mawu Ofanana  

Munthu akaikiza bulu, kapena ng'ombe, kapena nkhosa, kapena choweta china kwa mnansi wake, ndipo chikafa, kapena chiphwetekwa, kapena wina achipirikitsa osachiona munthu;


Agwire ntchito masiku asanu ndi limodzi; koma lachisanu ndi chiwiri ndilo Sabata lakupumula, lopatulika la Yehova; aliyense wogwira ntchito tsiku la Sabata aphedwe ndithu.


Masiku asanu ndi limodzi azigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri muliyese lopatulika, Sabata lakupuma la Yehova: aliyense agwira ntchito pamenepo, aphedwe.


Ukaletsa phazi lako pa Sabata, ndi kusiya kuchita kukondwerera kwako tsiku langa lopatulika, ndi kuyesa Sabata tsiku lokondwa lopatulika la Yehova, lolemekezeka, ndipo ukalilemekeza ilo, osachita njira zako zokha, osafuna kukondwa kwako kokha, osalankhula mau ako okha;


Koma Afarisi, pakuona, anati kwa Iye, Tapenyani, ophunzira anu achita chosaloleka tsiku la Sabata.


Ophunzira anu alumphiranji miyambo ya makolo? Pakuti sasamba manja pakudya.


Ndipo Afarisi ananena ndi Iye, Taona, achitiranji chosaloleka kuchitika tsiku la Sabata?


Ndipo iwo anati kwa Iye, Ophunzira a Yohane amasala kudya kawirikawiri, ndi kuchita mapemphero; chimodzimodzinso iwo a Afarisi; koma anu amangokudya ndi kumwa.


Ndipo chifukwa cha ichi Ayuda analondalonda Yesu, popeza anachita izo tsiku la Sabata.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa