Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 4:38 - Buku Lopatulika

38 Ndipo Iye ananyamuka kuchokera m'sunagoge, nalowa m'nyumba ya Simoni. Koma momwemo munali mpongozi wake wa Simoni, anagwidwa ndi nthenda yolimba yamalungo; ndipo anampempha Yesu za iye.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

38 Ndipo Iye ananyamuka kuchokera m'sunagoge, nalowa m'nyumba ya Simoni. Koma momwemo munali mpongozi wake wa Simoni, anagwidwa ndi nthenda yolimba yamalungo; ndipo anampempha Yesu za iye.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

38 Yesu adanyamuka nachoka ku nyumba yamapemphero kuja, nakaloŵa m'nyumba ya Simoni. Apongozi a Simoni ankadwala malungo aakulu, ndipo anthu adapempha Yesu kuti achitepo kanthu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.

Onani mutuwo Koperani




Luka 4:38
9 Mawu Ofanana  

Koma Iye sanamyankhe mau amodzi. Ndipo ophunzira ake anadza, nampempha, nati, Mumuuze amuke; pakuti afuula pambuyo pathu.


Ndipo mbiri yake inabuka ku Siriya konse: ndipo anatengera kwa Iye onse akudwala, ogwidwa ndi nthenda ndi mazunzo a mitundumitundu, ndi ogwidwa ndi ziwanda, ndi akhunyu, ndi amanjenje; ndipo Iye anawachiritsa.


Koma ngakhale tsopano ndidziwa kuti zinthu zilizonse mukapempha Mulungu, adzakupatsani Mulungu.


Pamenepo alongo ake anatumiza kwa Iye, nanena, Ambuye, onani, amene mumkonda adwala.


Kodi tilibe ulamuliro wakuyendayenda naye mkazi, ndiye mbale, monganso atumwi ena, ndi abale a Ambuye, ndi Kefa?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa