Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Luka 1:75 - Buku Lopatulika

75 m'chiyero ndi chilungamo pamaso pake, masiku athu onse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

75 m'chiyero ndi chilungamo pamaso pake, masiku athu onse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

75 kuti tikhale oyera mtima ndi olungama pamaso pake, masiku onse a moyo wathu.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

75 mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.

Onani mutuwo Koperani




Luka 1:75
19 Mawu Ofanana  

anthu amene ndinadzilengera ndekha, kuti aonetse matamando anga.


Atero Yehova wa makamu: Kusala kwa mwezi wachinai, ndi kusala kwa mwezi wachisanu, ndi kusala kwa mwezi wachisanu ndi chiwiri, ndi kusala kwa mwezi wakhumi kukhale kwa nyumba ya Yuda chimwemwe ndi chikondwerero, ndi nyengo zoikika zosekerera; chifukwa chake kondani choonadi ndi mtendere.


Ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake kumachimo ao.


Kutipatsa ife kuti titalanditsidwa kudzanja la adani athu, tidzamtumikira Iye, opanda mantha,


monga anatisankha ife mwa Iye, lisanakhazikike dziko lapansi, tikhale ife oyera mtima, ndi opanda chilema pamaso pake m'chikondi.


Pakuti ife ndife chipango chake, olengedwa mwa Khristu Yesu, kuchita ntchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo.


nimuvale munthu watsopano, amene analengedwa monga mwa Mulungu, m'chilungamo, ndi m'chiyero cha choonadi.


kuti muope Yehova Mulungu wanu, kusunga malemba ake onse ndi malamulo ake, amene ndikuuzani inu ndi ana anu, ndi zidzukulu zanu, masiku onse a moyo wanu, ndi kuti masiku anu achuluke.


Chotsalira tsono, abale, tikupemphani ndi kukudandaulirani mwa Ambuye Yesu, kuti, monga munalandira kwa ife mayendedwe okoma, muyenera kuyendanso ndi kukondweretsa Mulungu, monganso mumayenda, chulukani koposa momwemo.


Pakuti Mulungu sanaitane ife titsate chidetso, koma chiyeretso.


Koma tiyenera ife tiziyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu, abale okondedwa ndi Ambuye, kuti Mulungu anakusankhani inu kuyambira pachiyambi, mulandire chipulumutso mwa chiyeretso cha Mzimu ndi chikhulupiriro cha choonadi;


amene anatipulumutsa ife, natiitana ife ndi maitanidwe oyera, si monga mwa ntchito zathu, komatu monga mwa chitsimikizo mtima cha Iye yekha, ndi chisomo, chopatsika kwa ife mwa Khristu Yesu nthawi zisanayambe,


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa