Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Genesis 25:34 - Buku Lopatulika

34 Ndipo Yakobo anampatsa Esau mkate ndi mphodza zophika; ndipo iye anadya, namwa, nanyamuka, napita: chomwecho Esau ananyoza ukulu wake.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

34 Ndipo Yakobo anampatsa Esau mkate ndi mphodza zophika; ndipo iye anadya, namwa, nanyamuka, napita: chomwecho Esau ananyoza ukulu wake.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

34 Apo Yakobe adapatsa Esau buledi pamodzi ndi nyemba zija, ndipo Esau adadya namwera, kenaka adanyamuka nkuchokapo. Motero Esauyo adanyoza ukulu wake wauchisamba.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

34 Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita. Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.

Onani mutuwo Koperani




Genesis 25:34
15 Mawu Ofanana  

Ndipo Yakobo anaphika mphodza: ndipo Esau anachokera kuthengo, nalefuka:


Ndipo anati Yakobo, Undilumbirire ine lero lomwe, ndipo analumbirira iye; nagulana ndi Yakobo ukulu wake.


Ndipo panali njala padzikopo, yoyenjezeka ndi njala yoyamba ija imene inali masiku a Abrahamu, ndipo Isaki ananka kwa Abimeleki mfumu ya Afilisti ku Gerari.


Ndipo Isaki atate wake anati kwa iye, Ndiwe yani? Ndipo iye anati, Ndine mwana wanu woyamba Esau.


Anapeputsanso dziko lofunika, osavomereza mau ake;


Pompo ndinatama kusekaseka, pakuti munthu alibe kanthu kabwino pansi pano, koma kudya ndi kumwa, ndi kusekera; ndi kuti zimenezi zikhalebe naye m'vuto lake masiku onse a moyo wake umene Mulungu wampatsa pansi pano.


koma taonani, kukondwa, ndi kusekerera, ndi kupha ng'ombe, ndi kupha nkhosa, ndi kudya nyama, ndi kumwa vinyo; tiyeni tidye ndi kumwa, chifukwa mawa tidzafa.


Ndipo Yehova anati kwa ine, Kaziponye kwa woumba mbiya, mtengo wake wokometsetsa anandiyesawo. Ndipo ndinatenga masekeli makumi atatu a siliva, ndi kuziponya kwa woumba mbiya, m'nyumba ya Yehova.


Koma iwo ananyalanyaza, nachoka, wina kumunda wake, wina kumalonda ake:


nati, Mufuna kundipatsa chiyani, ndipo ine ndidzampereka Iye kwa inu? Ndipo iwo anamwerengera iye ndalama zasiliva makumi atatu.


Taonani, opeputsa inu, zizwani, kanganukani; kuti ndigwiritsa ntchito Ine masiku anu, ntchito imene simudzaikhulupirira wina akakuuzani.


Ngati ndinalimbana ndi zilombo ku Efeso monga mwa munthu, ndipindulanji? Ngati akufa saukitsidwa, tidye timwe pakuti mawa timwalira.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa