Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 9:17 - Buku Lopatulika

17 Kodi udzikwezanso pa anthu anga, ndi kusawalola amuke?

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

17 Kodi udzikwezanso pa anthu anga, ndi kusawalola amuke?

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

17 Koma ukunyozabe anthu anga, osafuna kuŵalola kuti apite.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

17 Komabe iwe ukudzitukumula pa anthu anga osawalola kuti atuluke.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 9:17
14 Mawu Ofanana  

Kodi uli nalo dzanja ngati Ine Mulungu? Kapena ukhoza kugunda ndi mau ngati Ine?


Ndiye wa mtima wanzeru, ndi wa mphamvu yaikulu; ndaniyo anadziumitsa mtima pa Iye, nakhala nao mtendere?


Koma ndithu chifukwa chake ndakuimika kuti ndikuonetse mphamvu yanga, ndi kuti alalikire dzina langa padziko lonse lapansi.


Taona, mawa monga nthawi ino ndidzavumbitsa mvumbi wa matalala, sipadakhale unzake mu Ejipito kuyambira tsiku lija lidakhazikika kufikira lero lino.


Kodi nkhwangwa idzadzikweza yokha, pa iye amene adula nayo? Kodi chochekera chidzadzikweza chokha pa iye amene achigwedeza, ngati chibonga ingamgwedeze iye amene ainyamula, ngati ndodo inganyamule kanthu popeza ili mtengo.


Yehova, dzanja lanu litukulidwa, koma iwo saona; koma iwo adzaona changu chanu cha kwa anthu, nadzakhala ndi manyazi; inde moto udzamaliza adani anu.


Chifukwa cha kundikwiyira Ine kwako, ndi popeza kudzikweza kwako kwafika m'makutu mwanga. Ine ndidzaika mbedza yanga m'mphuno mwako, ndi chapakamwa changa m'milomo yako, ndipo ndidzakubweza iwe m'njira yomwe unadzerayo.


Tsoka kwa iye amene akangana ndi Mlengi wake! Phale mwa mapale a dziko lapansi! Kodi dongo linganene kwa iye amene aliumba, Kodi upanga chiyani? Pena ntchito yako, Iye alibe manja?


chifukwa chake atero Ambuye Yehova, Popeza waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu;


Koma pokwezeka mtima wake, nulimba mzimu wake kuchita modzikuza, anamtsitsa pa mpando wa ufumu wake, namchotsera ulemerero wake;


Ndipo pomwepo mngelo wa Ambuye anamkantha, chifukwa sanampatse Mulungu ulemerero; ndipo anadyedwa ndi mphutsi, natsirizika.


Kapena kodi tichititsa nsanje Ambuye? Kodi mphamvu zathu ziposa Iye?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa