Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 7:14 - Buku Lopatulika

14 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Walemera mtima wa Farao, akana kulola anthu apite.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

14 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Walemera mtima wa Farao, akana kulola anthu apite.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

14 Tsono Chauta adauza Mose kuti, “Farao ndi wokanika kwambiri, akukana kulola anthu anga kuti apite.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

14 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Farao ndi wowuma mtima. Akukana kulola anthu anga kuti apite.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 7:14
21 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova anati kwa Mose, Lowa kwa Farao; pakuti ndaumitsa mtima wake, ndi mtima wa anyamata ake, kuti ndiike zizindikiro zanga izi pakati pao;


Koma Yehova analimbitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole ana a Israele amuke.


Koma Yehova analimbitsa mtima wake wa Farao, ndipo anakana kuwaleka amuke.


pakuti ukakana kulola anthu anga amuke, taona, mawa ndidzafikitsa dzombe m'dziko lako;


Koma Ine ndidziwa kuti mfumu ya Aejipito siidzalola inu kumuka, inde lingakhale ndi dzanja lamphamvu ai.


Ndipo ndanena ndi iwe, Mlole mwana wanga amuke, kuti anditumikire Ine; koma wakana kumlola kuti asamuke; taona, Ine ndidzamupha mwana wako wamwamuna, mwana wako woyamba.


Koma mtima wa Farao unalimba, ndipo sanamvere iwo; monga adalankhula Yehova.


Muka kwa Farao m'mawa; taona, atuluka kunka kumadzi; nuime kumlinda m'mbali mwa mtsinje; ndi ndodo idasanduka njokayo uigwire m'dzanja lako.


Ndipo achule adzachokera inu, ndi nyumba zanu, ndi anyamata anu, ndi anthu anu; adzatsala m'mtsinje mokha.


Koma pamene Farao anaona kuti panali kupuma, anaumitsa mtima wake, osamvera iwo; monga adalankhula Yehova.


Ndipo ukakana kuwalola amuke, taona, Ine ndidzapanda dziko lako lonse ndi achule;


Pakuti ukakana kuwalola amuke, ndi kuwagwira chigwiritsire,


Pamene Farao anaona kuti mvula ndi matalala ndi mabingu zidaleka anaonjezanso kuchimwa, naumitsa mtima wake, iye ndi anyamata ake.


Ndipo Farao anatuma, taonani, sichidafe chingakhale chimodzi chomwe cha zoweta za Aisraele. Koma mtima wa Farao unauma, ndipo sanalole anthu amuke.


koma ngati mukana ndi kupanduka, mudzathedwa ndi lupanga; chifukwa m'kamwa mwa Yehova mwatero.


Bwanji abwerera anthu awa a Yerusalemu chibwererere? Agwiritsa chinyengo, akana kubwera.


Ukhala pakati pa manyengo m'manyengo; akana kundidziwa, ati Yehova.


Inde, anasanduliza mitima yao ikhale ngati mwala woti gwaa, kuti angamve chilamulo, ndi mau amene Yehova wa makamu anatumiza ndi Mzimu wake mwa aneneri oyamba aja; m'menemo munafuma mkwiyo waukulu wochokera kwa Yehova wa makamu.


Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanatilole kupitira kwao; popeza Yehova Mulungu wanu anaumitsa mzimu wake, nalimbitsa mtima wake, kuti ampereke m'dzanja lanu, monga lero lino.


Penyani musakane wolankhulayo. Pakuti ngati iwowa sanapulumuke, pomkana Iye amene anawachenjeza padziko, koposatu sitidzapulumuka ife, odzipatulira kwa Iye wa Kumwamba;


Mulikuumitsiranji mitima yanu, monga Aejipito ndi Farao anaumitsa mitima yao? Kodi iwo sanalole anthuwo amuke, Iye atachita kodabwitsa pakati pao, ndipo anamuka?


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa