Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 39:43 - Buku Lopatulika

43 Ndipo Mose anaona ntchito zonse, ndipo, taonani, adaichita monga Yehova adamuuza, momwemo adachita. Ndipo Mose anawadalitsa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

43 Ndipo Mose anaona ntchito zonse, ndipo, taonani, adaichita monga Yehova adamuuza, momwemo adachita. Ndipo Mose anawadalitsa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

43 Tsono Mose adaona zonse zimene zidapangidwazo, ndipo adatsimikiza kuti adazipangadi monga momwe Chauta adalamulira. Pamenepo Mose adaŵadalitsa anthu onsewo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

43 Mose anayendera ntchitoyo ndipo anaona kuti anayichita monga momwe Yehova analamulira. Kotero Mose anawadalitsa.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 39:43
24 Mawu Ofanana  

Ndipo anaziona Mulungu zonse zimene adazipanga, ndipo, taonani, zinali zabwino ndithu. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.


Ndipo anamdalitsa iye, nati, Abramu adalitsike ndi Mulungu Wamkulukulu, mlengi wa kumwamba ndi dziko lapansi;


Pamene Davide adatsiriza kupereka nsembe yopsereza ndi zoyamika, iye anawadalitsa anthuwo m'dzina la Yehova wa makamu.


Ndipo m'chaka chakhumi ndi chimodzi m'mwezi wa Buli ndiwo mwezi wachisanu ndi chitatu anatsiriza nyumba konsekonse monga mwa mamangidwe ake onse. Momwemo anaimanga zaka zisanu ndi ziwiri.


Ndipo mfumu inapotoloka nkhope yake, nidalitsa msonkhano wonse wa Israele. Ndi msonkhano wonse wa Israele unaimirira.


Naimirira, nadalitsa msonkhano wonse wa Israele ndi mau okweza, nati,


Ndipo atatha Davide kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika, anadalitsa anthu m'dzina la Yehova.


Pamenepo ansembe Alevi anauka, nadalitsa anthu; ndi mau ao anamveka, ndi pemphero lao lidakwera pokhala pake popatulika Kumwamba.


Ndipo mfumu inapotolokera nkhope yake, nidalitsa khamu lonse la Israele; ndi khamu lonse la Israele linaimirira.


Ndipo anthu anadalitsa amuna onse akudzinenera mwaufulu kuti adzakhala mu Yerusalemu.


Ulemerero wa Yehova ukhale kosatha; Yehova akondwere mu ntchito zake;


Ndiponso kapolo wanu achenjezedwa nazo, m'kuzisunga izo muli mphotho yaikulu.


Ndipo anthu anawerama, nalambira. Ndipo ana a Israele anamuka nachita monga Yehova adalamulira Mose ndi Aroni; anachita momwemo.


Monga mwa zonse Ine ndilikuonetsa iwe, chifaniziro cha chihema, ndi chifaniziro cha zipangizo zake zonse, momwemo uchimange.


Monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, momwemo ana a Israele anachita ntchito zonse.


Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,


Nayatsa nyalizo pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.


Ndipo Mose ndi Aroni anachita monga Yehova anawalamulira, momwemo anachita.


Ndipo ndinapita, ndinaubisa pa Yufurate, monga Yehova anandiuza ine.


Ndipo ichi chikhale kwa inu lemba losatha, kuchita chotetezera ana a Israele, chifukwa cha zochimwa zao zonse, kamodzi chaka chimodzi. Ndipo anachita monga Yehova adauza Mose.


Momwemo Yoswa anawadalitsa, nawauza amuke; ndipo anamuka ku mahema ao.


Ndipo gawo limodzi la fuko la Manase, Mose anawapatsa cholowa mu Basani; koma gawo lina Yoswa anawaninkha cholowa pakati pa abale ao tsidya lija la Yordani kumadzulo. Ndiponso pamene Yoswa anawauza amuke ku mahema ao, anawadalitsa;


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa