Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 39:42 - Buku Lopatulika

42 Monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, momwemo ana a Israele anachita ntchito zonse.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

42 Monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, momwemo ana a Israele anachita ntchito zonse.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

42 Motero Aisraele adachitadi ntchito zonse, monga momwe Chauta adalamulira Mose.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

42 Aisraeli anagwira ntchito yonse monga momwe Yehova analamulira Mose.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 39:42
15 Mawu Ofanana  

Ndipo m'chaka chakhumi ndi chimodzi m'mwezi wa Buli ndiwo mwezi wachisanu ndi chitatu anatsiriza nyumba konsekonse monga mwa mamangidwe ake onse. Momwemo anaimanga zaka zisanu ndi ziwiri.


Ndipo sanapatuke pa lamulo la mfumu la kwa ansembe ndi Alevi, kunena za kanthu kalikonse, kapena za chumachi.


Ndipo anthu anawerama, nalambira. Ndipo ana a Israele anamuka nachita monga Yehova adalamulira Mose ndi Aroni; anachita momwemo.


Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova analamula;


Potero anatsiriza ntchito yonse ya Kachisi wa chihema chokomanako; ndipo ana a Israele adachita monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, anachita momwemo.


zovala zokoma za kutumikira nazo m'malo opatulika, ndi zovala zopatulika za Aroni wansembe, ndi zovala za ana ake, kuchita nazo ntchito ya nsembe.


Ndipo Mose anaona ntchito zonse, ndipo, taonani, adaichita monga Yehova adamuuza, momwemo adachita. Ndipo Mose anawadalitsa.


Ndipo ndinapita, ndinaubisa pa Yufurate, monga Yehova anandiuza ine.


Ngakhale masiku awiri, kapena mwezi, kapena masiku ambiri, pokhalitsa mtambo pamwamba pa chihema ndi kukhalapo, ana a Israele anakhala m'chigono, osayenda ulendo; koma pakukwera uwu, anayenda ulendo.


ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulani inu; ndipo onani, Ine ndili pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira chimaliziro cha nthawi ya pansi pano.


Chilichonse ndikuuzani, muchisamalire kuchichita; musamaonjezako, kapena kuchepsako.


Uchite changu kudzionetsera kwa Mulungu wovomerezeka, wantchito wopanda chifukwa cha kuchita manyazi, wolunjika nao bwino mau a choonadi.


Ndalimbana nako kulimbana kwabwino, ndatsiriza njirayo, ndasunga chikhulupiriro:


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa