Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 24:11 - Buku Lopatulika

11 Koma sanatulutse dzanja lake pa akulu a ena a Israele; ndipo anapenya Mulungu, nadya, namwa.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

11 Koma sanatulutse dzanja lake pa akulu a ena a Israele; ndipo anapenya Mulungu, nadya, namwa.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

11 Mulungu sadaŵaononge atsogoleri a Aisraelewo. Iwowo adampenyadi Mulungu, kenaka adadya ndi kumwa.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

11 Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 24:11
24 Mawu Ofanana  

Ndipo anatcha dzina la Yehova amene ananena naye, Ndinu Mulungu wakundiona ine; pakuti anati, Kodi kunonso ndayang'ana pambuyo pake pa Iye amene wakundiona ine?


Pakuti Abrahamu adzakhala ndithu wamkulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya dziko lapansi idzadalitsika mwa iye?


Ndipo Yakobo anapereka nsembe paphiripo, naitana abale ake kuti adye chakudya; ndipo anadya chakudya, nagona paphiripo usiku wonse.


M'mwemo analemba makalata m'dzina la Ahabu nakhomerapo chizindikiro chake, natumiza makalatawo kwa akulu ndi omveka anali m'mzinda mwake, nakhala naye, Naboti.


Natenga atsogoleri a mazana, ndi omveka, ndi akazembe a anthu, ndi anthu onse a m'dziko, natsika ndi mfumu kunyumba ya Yehova; nalowera pa chipata cha kumtunda m'nyumba ya mfumu, namkhalitsa mfumu pa mpando wa ufumu.


Koma olamulira sanadziwe uko ndinamuka, kapena chochita ine; sindidauzenso kufikira pamenepo Ayuda, kapena ansembe, kapena aufulu, kapena olamulira, kapena otsala akuchita ntchitoyi.


Munandizinga kumbuyo ndi kumaso, nimunaika dzanja lanu pa ine.


Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose, anamtengera Mulungu nsembe yopsereza, ndi nsembe zophera; ndipo Aroni ndi akulu onse a Israele anadza kudzadya mkate ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tsika, chenjeza anthu, kuti angapyolere kwa Yehova kudzaona, ndipo angagwe ambiri a iwowa.


Ndipo Iye ananena ndi Mose, Ukwere kudza kwa Yehova, iwe ndi Aroni, Nadabu ndi Abihu, ndi akulu a Israele makumi asanu ndi awiri; ndipo mugwadire pakudza kutali;


Tiye, idya zakudya zako mokondwa, numwe vinyo wako mosekera mtima; pakuti Mulungu wavomerezeratu zochita zako.


Akulu ao atuma ang'ono ao kumadzi; afika kumaenje, osapeza madzi; abwera ndi mitsuko yao yopanda kanthu; ali ndi manyazi, athedwa nzeru, afunda mitu yao.


Pakuti mnyamata wa mbuye wanga inu akhoza bwanji kulankhula ndi mbuye wanga inu? Pakuti ine tsopano apa mulibenso mphamvu mwa ine, osanditsaliranso mpweya.


Ndimanena naye pakamwa ndi pakamwa, moonekera, osati mophiphiritsa; ndipo amapenyerera maonekedwe a Yehova; potero munalekeranji kuopa kutsutsana naye mtumiki wanga, Mose.


chitsime adakumba mafumu, adachikonza omveka a anthu; atanena mlamuli, ndi ndodo zao. Ndipo atachoka kuchipululu anamuka ku Matana;


ndipo kumeneko muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kukondwera nazo zonse mudazigwira ndi dzanja lanu, inu ndi a pa banja lanu, m'mene Yehova Mulungu wanu anakudalitsani.


Kodi pali mtundu wa anthu udamva mau a mulungu wina akunena pakati pa moto, monga mudamva inu, ndi kukhala ndi moyo?


Nati Manowa kwa mkazi wake, Tidzafa ndithu pakuti taona Mulungu.


Pamenepo omveka otsala anatsika ndi anthu; Yehova ananditsikira pakati pa achamuna.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa