Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 22:18 - Buku Lopatulika

18 Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

18 Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

18 “Munthu wamkazi wochita zaufiti, musamlole kuti akhale moyo.

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

18 “Musayilole mfiti yayikazi kuti ikhale ndi moyo.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 22:18
17 Mawu Ofanana  

Ndipo mzimu wa Ejipito adzakhala wachabe pakati pake; ndipo Ine ndidzaononga uphungu wake; ndimo iwo adzafunafuna mafano ndi anyanga, ndi alauli, ndi obwebweta.


pakuti iwo akunenerani inu zonama, kuti akuchotseni inu m'dziko lanu, kunka kutali kuti ndikupirikitseni inu, ndipo inu mudzathedwa.


Koma inu, musamvere aneneri anu, kapena akuombeza anu, kapena maloto anu, kapena alauli anu, kapena obwebweta anu, Musadzatumikira mfumu ya ku Babiloni;


Ndipo usamagonana ndi nyama iliyonse, kudetsedwa nayo; kapena mkazi asamaima panyama, kugonana nayo; chisokonezo choopsa ichi.


Musamadya kanthu ndi mwazi wake; musamachita nyanga, kapena kuombeza ula.


Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.


Munthu wamwamuna kapena wamkazi wakubwebweta, kapena wanyanga, azimupha ndithu; aziwaponya miyala; mwazi wao ukhale pamutu pao.


Ndipo munthu wakutembenukira kwa obwebweta ndi anyanga kuwatsata ndi chigololo, nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndipo ndidzamsadza kumchotsa pakati pa anthu a mtundu wake.


Ndipo ambiri a iwo akuchita zamatsenga anasonkhanitsa mabuku ao, nawatentha pamaso pa onse; ndipo anawerenga mtengo wake, napeza ndalama zasiliva zikwi makumi asanu.


kupembedza mafano, nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko,


Wotembereredwa iye wakugona ndi nyama iliyonse. Ndi anthu onse anene, Amen.


Kunja kuli agalu ndi anyanga, ndi achigololo, ndi ambanda, ndi opembedza mafano, ndi yense wakukonda bodza ndi kulichita.


M'menemo Samuele ndipo atafa, ndipo Aisraele onse atalira maliro ake, namuika mu Rama, m'mzinda mwao. Ndipo Saulo anachotsa m'dzikomo obwebweta onse, ndi aula onse.


Ndipo mkaziyo ananena naye, Onani, mudziwa chimene anachita Saulo, kuti analikha m'dzikomo obwebweta onse, ndi aula; chifukwa ninji tsono mulikutchera moyo wanga msampha, kundifetsa.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa