Biblia Todo Logo
Baibulo la pa intaneti
- Zotsatsa -




Eksodo 20:16 - Buku Lopatulika

16 Usamnamizire mnzako.

Onani mutuwo Koperani

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

16 Usamnamizire mnzako.

Onani mutuwo Koperani

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

16 “Usachite umboni womnamizira mnzako.”

Onani mutuwo Koperani

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

16 “Usapereke umboni womunamizira mnzako.

Onani mutuwo Koperani




Eksodo 20:16
23 Mawu Ofanana  

Amene sasinjirira ndi lilime lake, nachitira mnzake choipa, ndipo satola miseche pa mnansi wake.


Usatola mbiri yopanda pake; usathandizana naye woipa ndi kukhala mboni yochititsa chiwawa.


Wobisa udani ali ndi milomo yonama; wonena ugogodi ndiye chitsiru.


Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi; koma wokhulupirika mtima abisa mau.


Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa; wolankhula mabodza sadzapulumuka.


Wochitira mnzake umboni wonama ndiye chibonga, ndi lupanga, ndi muvi wakuthwa.


Musamaba, kapena kunyenga, kapena kunamizana.


Usamayendayenda nusinjirira mwa anthu a mtundu wako; usamatsata mwazi wa mnansi wako; Ine ndine Yehova.


Usamabwezera chilango, kapena kusunga kanthu kukhosi pa ana a anthu a mtundu wako; koma uzikonda mnansi wako monga udzikonda wekha; Ine ndine Yehova.


Iye ananena kwa Iye, Otani? Ndipo Yesu anati, Usaphe, Usachite chigololo, Usabe, Usachite umboni wonama,


Ndipo asilikali omwe anamfunsa iye, nati, Nanga ife tizichita chiyani? Ndipo iye anati kwa iwo, Musaopse, musanamize munthu aliyense; khalani okhuta ndi kulipira kwanu.


naimika mboni zonama, zakunena, Munthu ameneyo saleka kunenera malo oyera amene, ndi chilamulo;


Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse.


achigololo, akuchita zoipa ndi amuna, akuba anthu, amabodza, olumbira zonama, ndipo ngati kuli kena kakutsutsana nacho chiphunzitso cholamitsa;


osayera mtima, opanda chikondi chachibadwidwe, osayanjanitsika, akudierekeza, osakhoza kudziletsa, aukali, osakonda abwino,


Musamanenerana, abale. Wonenera mbale, kapena woweruza mbale wake, anenera lamulo, naweruza lamulo: koma ngati uweruza lamulo, suli wochita lamulo, komatu woweruza.


Titsatireni:

Zotsatsa


Zotsatsa