Eksodo 13:9 - Buku Lopatulika9 Ndipo chizikhala ndi iwe ngati chizindikiro padzanja lako, ndi chikumbutso pakati pamaso ako; kuti chilamulo cha Yehova chikhale m'kamwa mwako; pakuti Yehova anakutulutsa mu Ejipito ndi dzanja lamphamvu. Onani mutuwoChichewa Buku Lopatulika Bible 20149 Ndipo chizikhala ndi iwe ngati chizindikiro pa dzanja lako, ndi chikumbutso pakati pa maso ako; kuti chilamulo cha Yehova chikhale m'kamwa mwako; pakuti Yehova anakutulutsa m'Ejipito ndi dzanja lamphamvu. Onani mutuwoBuku Loyera Catholic Edition - Chichewa9 Lamulo limeneli lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa padzanja panu, kapena chikumbutso chomangidwa pamphumi panu. Motero malamulo a Chauta sadzachoka konse pakamwa panu, chifukwa Iye adakutulutsani ku Ejipito ndi dzanja lake lamphamvu. Onani mutuwoMawu a Mulungu mu Chichewa Chalero9 Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu. Onani mutuwo |